< Psalms 83 >

1 A song, or Psalme committed to Asaph. Keep not thou silence, O God: bee not still, and cease not, O God.
Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
2 For lo, thine enemies make a tumult: and they that hate thee, haue lifted vp the head.
Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
3 They haue taken craftie counsell against thy people, and haue consulted against thy secret ones.
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
4 They haue said, Come and let vs cut them off from being a nation: and let the name of Israel be no more in remembrance.
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
5 For they haue consulted together in heart, and haue made a league against thee:
Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
6 The tabernacles of Edom, and the Ishmaelites, Moab and the Agarims:
Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
7 Gebal and Ammon, and Amalech, the Philistims with the inhabitants of Tyrus:
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
8 Asshur also is ioyned with them: they haue bene an arme to the children of Lot. (Selah)
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
9 Doe thou to them as vnto the Midianites: as to Sisera and as to Iabin at the riuer of Kishon.
Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
10 They perished at En-dor, and were dung for the earth.
Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
11 Make them, euen their princes like Oreb and like Zeeb: yea, all their princes like Zebah and like Zalmuna.
Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
12 Which haue said, Let vs take for our possession the habitations of God.
amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
13 O my God, make them like vnto a wheele, and as the stubble before the winde.
Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
14 As the fire burneth the forest, and as the flame setteth the mountaines on fire:
Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
15 So persecute them with thy tempest, and make them afraide with thy storme.
kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
16 Fill their faces with shame, that they may seeke thy Name, O Lord.
Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
17 Let them be confounded and troubled for euer: yea, let them be put to shame and perish,
Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
18 That they may knowe that thou, which art called Iehouah, art alone, euen the most High ouer all the earth.
Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

< Psalms 83 >