< Psalms 82 >

1 A Psalme committed to Aspah. God standeth in the assemblie of gods: hee iudgeth among gods.
Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2 How long wil ye iudge vniustly, and accept the persons of the wicked? (Selah)
“Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
3 Doe right to the poore and fatherlesse: doe iustice to the poore and needie.
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4 Deliuer the poore and needie: saue them from the hand of the wicked.
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
5 They knowe not and vnderstand nothing: they walke in darkenes, albeit all the foundations of the earth be mooued.
“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6 I haue said, Ye are gods, and ye all are children of the most High.
“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7 But ye shall die as a man, and yee princes, shall fall like others.
Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
8 O God, arise, therefore iudge thou the earth: for thou shalt inherite all nations.
Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

< Psalms 82 >