< Psalms 75 >

1 To him that excelleth. Destroy not. A Psalme or song committed toAsaph. We will prayse thee, O God, we will prayse thee, for thy Name is neere: therefore they will declare thy wonderous workes.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 When I shall take a conuenient time, I will iudge righteously.
Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 The earth and all the inhabitantes thereof are dissolued: but I will establish the pillars of it. (Selah)
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
4 I saide vnto the foolish, Be not so foolish, and to the wicked, Lift not vp the horne.
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Lift not vp your horne on high, neither speake with a stiffe necke.
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
6 For to come to preferment is neither from the East, nor from the West, nor from the South,
Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
7 But God is the iudge: he maketh lowe and he maketh hie.
Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 For in the hand of the Lord is a cup, and the wine is red: it is full mixt, and he powreth out of the same: surely all the wicked of the earth shall wring out and drinke the dregges thereof.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
9 But I will declare for euer, and sing prayses vnto the God of Iaakob.
Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 All the hornes of the wicked also will I breake: but the hornes of the righteous shalbe exalted.
Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

< Psalms 75 >