< Psalms 70 >

1 To him excelleth. A Psalme of David to put in remembrance. O God, haste thee to deliuer mee: make haste to helpe me, O Lord.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho. Fulumirani Mulungu kundipulumutsa; Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
2 Let them be confounded and put to shame, that seeke my soule: let them bee turned backewarde and put to rebuke, that desire mine hurt.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene akukhumba chiwonongeko changa abwezedwe mopanda ulemu.
3 Let them be turned backe for a rewarde of their shame, which said, Aha, aha.
Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,” abwerere chifukwa cha manyazi awo.
4 But let all those that seeke thee, be ioyfull and glad in thee, and let all that loue thy saluation, say alwaies, God be praised.
Koma onse amene akufunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”
5 Nowe I am poore and needie: O God, make haste to me: thou art mine helper, and my deliuerer: O Lord, make no tarying.
Koma ine ndine wosauka ndi wosowa; bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu. Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga; Inu Yehova musachedwe.

< Psalms 70 >