< Psalms 63 >

1 A Psalme of David. When he was in the wildernesse of Judah. O God, thou art my God, earely will I seeke thee: my soule thirsteth for thee: my flesh longeth greatly after thee in a barren and drye land without water.
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 Thus I beholde thee as in the Sanctuarie, when I beholde thy power and thy glorie.
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 For thy louing kindnesse is better then life: therefore my lippes shall prayse thee.
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 Thus will I magnifie thee all my life, and lift vp mine hands in thy name.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 My soule shalbe satisfied, as with marowe and fatnesse, and my mouth shall praise thee with ioyfull lippes,
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 When I remember thee on my bedde, and when I thinke vpon thee in the night watches.
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 Because thou hast bene mine helper, therefore vnder the shadow of thy wings wil I reioyce.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 My soule cleaueth vnto thee: for thy right hand vpholdeth me.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 Therefore they that seeke my soule to destroy it, they shall goe into the lowest partes of the earth.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 They shall cast him downe with the edge of the sword, and they shall be a portion for foxes.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 But the King shall reioyce in God, and all that sweare by him shall reioyce in him: for the mouth of them that speake lyes, shall be stopped.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

< Psalms 63 >