< Psalms 60 >
1 To him that excelleth upon Shushan Eduth, or Michtam. A Psalme of David to teach. When he fought against Aram Naharaim, and against Aram Zobah, when Joab returned and slew twelve thousand Edomites in the salt valley. O God, thou hast cast vs out, thou hast scattered vs, thou hast bene angry, turne againe vnto vs.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 Thou hast made the land to tremble, and hast made it to gape: heale the breaches thereof, for it is shaken.
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Thou hast shewed thy people heauy things: thou hast made vs to drinke the wine of giddines.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 But now thou hast giuen a banner to them that feare thee, that it may be displayed because of thy trueth. (Selah)
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 That thy beloued may be deliuered, helpe with thy right hand and heare me.
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 God hath spoken in his holines: therefore I will reioyce: I shall deuide Shechem, and measure the valley of Succoth.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Gilead shalbe mine, and Manasseh shalbe mine: Ephraim also shalbe the strength of mine head: Iudah is my lawgiuer.
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab shalbe my wash pot: ouer Edom will I cast out my shoe: Palestina shew thy selfe ioyfull for me.
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Who will leade me into the strong citie? who will bring me vnto Edom?
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Wilt not thou, O God, which hadest cast vs off, and didest not go forth, O God, with our armies?
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Giue vs helpe against trouble: for vaine is the helpe of man.
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 Through God we shall doe valiantly: for he shall tread downe our enemies.
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.