< Psalms 58 >
1 To him that excelleth. Destroy not. A Psalme of David on Michtam. Is it true? O Congregation, speake ye iustly? O sonnes of men, iudge ye vprightly?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
2 Yea, rather ye imagine mischiefe in your heart: your hands execute crueltie vpon the earth.
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
3 The wicked are strangers from ye wombe: euen from the belly haue they erred, and speake lyes.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
4 Their poyson is euen like the poyson of a serpent: like ye deafe adder that stoppeth his eare.
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
5 Which heareth not the voyce of the inchanter, though he be most expert in charming.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
6 Breake their teeth, O God, in their mouthes: breake the iawes of the yong lions, O Lord.
Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
7 Let them melt like the waters, let them passe away: when hee shooteth his arrowes, let them be as broken.
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
8 Let them consume like a snayle that melteth, and like the vntimely fruite of a woman, that hath not seene the sunne.
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
9 As raw flesh before your pots feele the fire of thornes: so let him cary them away as with a whirlewinde in his wrath.
Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 The righteous shall reioyce when he seeeth the vengeance: he shall wash his feete in the blood of the wicked.
Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 And men shall say, Verily there is fruite for the righteous: doutlesse there is a God that iudgeth in the earth.
Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”