< Psalms 54 >
1 To him that excelleth on Neginoth. A Psalme of David, to give instruction. When the Ziphims came and said unto Saul, Is not David hid among us? Save mee, O God, by thy Name, and by thy power iudge me.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2 O God, heare my prayer: hearken vnto the wordes of my mouth.
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
3 For strangers are risen vp against me, and tyrants seeke my soule: they haue not set God before them. (Selah)
Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
4 Beholde, God is mine helper: the Lord is with them that vpholde my soule.
Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5 He shall rewarde euill vnto mine enemies: Oh cut them off in thy trueth!
Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6 Then I will sacrifice freely vnto thee: I wil praise thy Name, O Lord, because it is good.
Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
7 For he hath deliuered me out of al trouble, and mine eye hath seene my desire vpon mine enemies.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.