< Psalms 51 >

1 To him that excelleth. A Psalme of David, when the Prophet Nathan came unto him, after he had gone in to Bath-sheba. Have mercie vpon me, O God, according to thy louing kindnes: according to the multitude of thy compassions put away mine iniquities.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
2 Wash me throughly from mine iniquitie, and clense me from my sinne.
Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
3 For I know mine iniquities, and my sinne is euer before me.
Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
4 Against thee, against thee onely haue I sinned, and done euill in thy sight, that thou mayest be iust when thou speakest, and pure when thou iudgest.
Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
5 Beholde, I was borne in iniquitie, and in sinne hath my mother conceiued me.
Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
6 Beholde, thou louest trueth in the inwarde affections: therefore hast thou taught mee wisedome in the secret of mine heart.
Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
7 Purge me with hyssope, and I shalbe cleane: wash me, and I shalbe whiter then snowe.
Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
8 Make me to heare ioye and gladnes, that the bones, which thou hast broken, may reioyce.
Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
9 Hide thy face from my sinnes, and put away all mine iniquities.
Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
10 Create in mee a cleane heart, O God, and renue a right spirit within me.
Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
11 Cast mee not away from thy presence, and take not thine holy Spirit from me.
Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
12 Restore to me the ioy of thy saluation, and stablish me with thy free Spirit.
Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
13 Then shall I teache thy wayes vnto the wicked, and sinners shalbe conuerted vnto thee.
Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
14 Deliuer me from blood, O God, which art the God of my saluation, and my tongue shall sing ioyfully of thy righteousnes.
Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
15 Open thou my lippes, O Lord, and my mouth shall shewe foorth thy praise.
Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
16 For thou desirest no sacrifice, though I would giue it: thou delitest not in burnt offering.
Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
17 The sacrifices of God are a contrite spirit: a contrite and a broken heart, O God, thou wilt not despise.
Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
18 Bee fauourable vnto Zion for thy good pleasure: builde the walles of Ierusalem.
Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
19 Then shalt thou accept ye sacrifices of righteousnes, euen the burnt offering and oblation: then shall they offer calues vpon thine altar.
Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.

< Psalms 51 >