< Psalms 50 >

1 A Psalme of Asaph. The God of Gods, euen the Lord hath spoken and called the earth from the rising vp of the sunne vnto the going downe thereof.
Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
2 Out of Zion, which is the perfection of beautie, hath God shined.
Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
3 Our God shall come and shall not keepe silence: a fire shall deuoure before him, and a mightie tempest shall be mooued round about him.
Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
4 Hee shall call the heauen aboue, and the earth to iudge his people.
Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
5 Gather my Saints together vnto me, those that make a couenant with me with sacrifice.
Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
6 And the heauens shall declare his righteousnes: for God is iudge himselfe. (Selah)
Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
7 Heare, O my people, and I wil speake: heare, O Israel, and I wil testifie vnto thee: for I am God, euen thy God.
Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
8 I wil not reproue thee for thy sacrifices, or thy burnt offerings, that haue not bene continually before me.
Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
9 I will take no bullocke out of thine house, nor goates out of thy foldes.
Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
10 For all the beastes of the forest are mine, and the beastes on a thousand mountaines.
pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
11 I knowe all the foules on the mountaines: and the wilde beastes of the fielde are mine.
Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
12 If I bee hungry, I will not tell thee: for the world is mine, and all that therein is.
Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
13 Will I eate the flesh of bulles? or drinke the blood of goates?
Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
14 Offer vnto God praise, and pay thy vowes vnto the most High,
“Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
15 And call vpon me in the day of trouble: so will I deliuer thee, and thou shalt glorifie me.
Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
16 But vnto the wicked said God, What hast thou to doe to declare mine ordinances, that thou shouldest take my couenant in thy mouth,
Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
17 Seeing thou hatest to bee reformed, and hast cast my wordes behinde thee?
Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
18 For when thou seest a thiefe, thou runnest with him, and thou art partaker with the adulterers.
Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
19 Thou giuest thy mouth to euill, and with thy tongue thou forgest deceit.
Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
20 Thou sittest, and speakest against thy brother, and slanderest thy mothers sonne.
Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
21 These things hast thou done, and I held my tongue: therefore thou thoughtest that I was like thee: but I will reproue thee, and set them in order before thee.
Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
22 Oh cosider this, ye that forget God, least I teare you in pieces, and there be none that can deliuer you.
“Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 He that offereth praise, shall glorifie mee: and to him, that disposeth his way aright, will I shew the saluation of God.
Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”

< Psalms 50 >