< Psalms 49 >

1 To him that excelleth. A Psalme committed to the sonnes of Korah. Heare this, all ye people: giue eare, all ye that dwell in the world,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
2 As well lowe as hie, both rich and poore.
anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
3 My mouth shall speake of wisdome, and the meditation of mine heart is of knowledge.
Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
4 I will incline mine eare to a parable, and vtter my graue matter vpon the harpe.
Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
5 Wherefore should I feare in the euil dayes, when iniquitie shall compasse me about, as at mine heeles?
Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
6 They trust in their goods, and boast them selues in the multitude of their riches.
Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
7 Yet a man can by no meanes redeeme his brother: he can not giue his raunsome to God,
Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
8 (So precious is the redemption of their soules, and the continuance for euer)
Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
9 That he may liue still for euer, and not see the graue.
kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
10 For he seeth that wise men die, and also that the ignorant and foolish perish, and leaue their riches for others.
Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
11 Yet they thinke, their houses, and their habitations shall continue for euer, euen from generation to generation, and call their lands by their names.
Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
12 But man shall not continue in honour: he is like the beastes that die.
Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
13 This their way vttereth their foolishnes: yet their posteritie delite in their talke. (Selah)
Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
14 Like sheepe they lie in graue: death deuoureth them, and the righteous shall haue domination ouer them in the morning: for their beautie shall consume, when they shall goe from their house to graue. (Sheol h7585)
Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
15 But God shall deliuer my soule from the power of the graue: for he will receiue me. (Selah) (Sheol h7585)
Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
16 Be not thou afrayd when one is made rich, and when the glory of his house is increased.
Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
17 For he shall take nothing away when he dieth, neither shall his pompe descende after him.
Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
18 For while he liued, he reioyced himselfe: and men will prayse thee, when thou makest much of thy selfe.
Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
19 He shall enter into the generation of his fathers, and they shall not liue for euer.
iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
20 Man is in honour, and vnderstandeth not: he is like to beasts that perish.
Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.

< Psalms 49 >