< Psalms 48 >
1 A song or Psalme committed to the sonnes of Korah. Great is the Lord, and greatly to be praysed, in the Citie of our God, euen vpon his holy Mountaine.
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 Mount Zion, lying Northwarde, is faire in situation: it is the ioy of the whole earth, and the Citie of the great King.
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 In the palaces thereof God is knowen for a refuge.
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 For lo, the Kings were gathered, and went together.
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 When they sawe it, they marueiled: they were astonied, and suddenly driuen backe.
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
6 Feare came there vpon them, and sorowe, as vpon a woman in trauaile.
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 As with an East winde thou breakest the shippes of Tarshish, so were they destroyed.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 As we haue heard, so haue we seene in the citie of the Lord of hostes, in the Citie of our God: God will stablish it for euer. (Selah)
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 We waite for thy louing kindnes, O God, in the middes of thy Temple.
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 O God, according vnto thy Name, so is thy prayse vnto the worlds end: thy right hand is full of righteousnes.
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 Let mount Zion reioyce, and the daughters of Iudah be glad, because of thy iudgements.
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
12 Compasse about Zion, and goe round about it, and tell the towres thereof.
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
13 Marke well the wall thereof: beholde her towres, that ye may tell your posteritie.
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 For this God is our God for euer and euer: he shall be our guide vnto the death.
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.