< Psalms 43 >

1 Judge me, O God, and defend my cause against the vnmercifull people: deliuer mee from the deceitfull and wicked man.
Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 For thou art the God of my strength: why hast thou put me away? why goe I so mourning, when the enemie oppresseth me?
Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
3 Sende thy light and thy trueth: let them leade mee: let them bring mee vnto thine holy Mountaine and to thy Tabernacles.
Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
4 Then wil I go vnto the altar of God, euen vnto the God of my ioy and gladnes: and vpon the harpe wil I giue thanks vnto thee, O God, my God.
Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
5 Why art thou cast downe, my soule? and why art thou disquieted within mee? waite on God: for I will yet giue him thankes, he is my present helpe, and my God.
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

< Psalms 43 >