< Psalms 34 >

1 A Psalme of Dauid, when he changed his behauiour before Abimelech, who droue him away, and he departed. I will alway giue thankes vnto the Lord: his praise shalbe in my mouth continually.
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 My soule shall glory in the Lord: the humble shall heare it, and be glad.
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 Praise ye the Lord with me, and let vs magnifie his Name together.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 I sought the Lord, and he heard me: yea, he deliuered me out of all my feare.
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 They shall looke vnto him, and runne to him: and their faces shall not be ashamed, saying,
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 This poore man cryed, and the Lord heard him, and saued him out of all his troubles.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 The Angel of the Lord pitcheth round about them, that feare him, and deliuereth them.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 Taste ye and see, howe gratious the Lord is: blessed is the man that trusteth in him.
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 Feare the Lord, ye his Saintes: for nothing wanteth to them that feare him.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 The lyons doe lacke and suffer hunger, but they, which seeke the Lord, shall want nothing that is good.
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Come children, hearken vnto me: I will teache you the feare of the Lord.
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 What man is he, that desireth life, and loueth long dayes for to see good?
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 Keepe thy tongue from euill, and thy lips, that they speake no guile.
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Eschewe euill and doe good: seeke peace and follow after it.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 The eyes of the Lord are vpon the righteous, and his eares are open vnto their crie.
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 But the face of the Lord is against them that doe euill, to cut off their remembrance from the earth.
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 The righteous crie, and the Lord heareth them, and deliuereth them out of all their troubles.
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 The Lord is neere vnto them that are of a contrite heart, and will saue such as be afflicted in Spirite.
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 Great are the troubles of the righteous: but the Lord deliuereth him out of them all.
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 He keepeth all his bones: not one of them is broken.
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 But malice shall slay the wicked: and they that hate the righteous, shall perish.
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 The Lord redeemeth the soules of his seruants: and none, that trust in him, shall perish.
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.

< Psalms 34 >