< Psalms 31 >
1 To him that excelleth. A Psalme of David. In thee, O Lord, haue I put my trust: let mee neuer be confounded: deliuer me in thy righteousnesse.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
2 Bowe downe thine eare to me: make haste to deliuer mee: be vnto me a stronge rocke, and an house of defence to saue me.
Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
3 For thou art my rocke and my fortresse: therefore for thy Names sake direct mee and guide me.
Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
4 Drawe mee out of the nette, that they haue layde priuilie for mee: for thou art my strength.
Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
5 Into thine hand I commend my spirit: for thou hast redeemed me, O Lord God of trueth.
Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
6 I haue hated them that giue them selues to deceitfull vanities: for I trust in the Lord.
Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
7 I wil be glad and reioyce in thy mercie: for thou hast seene my trouble: thou hast knowen my soule in aduersities,
Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
8 And thou hast not shut me vp in the hand of the enemie, but hast set my feete at large.
Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
9 Haue mercie vpon mee, O Lord: for I am in trouble: mine eye, my soule and my bellie are consumed with griefe.
Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
10 For my life is wasted with heauinesse, and my yeeres with mourning: my strength faileth for my paine, and my bones are consumed.
Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
11 I was a reproch among all mine enemies, but specially among my neighbours: and a feare to mine acquaintance, who seeing me in the streete, fled from me.
Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
12 I am forgotten, as a dead man out of minde: I am like a broken vessell.
Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
13 For I haue heard the rayling of great men: feare was on euery side, while they conspired together against mee, and consulted to take my life.
Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
14 But I trusted in thee, O Lord: I said, Thou art my God.
Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
15 My times are in thine hande: deliuer mee from the hande of mine enemies, and from them that persecute me.
Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
16 Make thy face to shine vpon thy seruant, and saue me through thy mercie.
Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
17 Let me not be confounded, O Lord: for I haue called vpon thee: let the wicked bee put to confusion, and to silence in the graue. (Sheol )
Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol )
18 Let the lying lips be made dumme, which cruelly, proudly and spitefully speake against the righteous.
Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
19 Howe great is thy goodnesse, which thou hast layde vp for them, that feare thee! and done to them, that trust in thee, euen before the sonnes of men!
Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
20 Thou doest hide them priuily in thy presence from the pride of men: thou keepest them secretly in thy Tabernacle from the strife of tongues.
Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
21 Blessed be the Lord: for hee hath shewed his marueilous kindenesse toward me in a strong citie.
Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
22 Though I said in mine haste, I am cast out of thy sight, yet thou heardest the voyce of my prayer, when I cryed vnto thee.
Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
23 Loue ye the Lord all his Saintes: for the Lord preserueth the faithfull, and rewardeth abundantly the proud doer.
Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
24 All ye that trust in the Lord, be strong, and he shall establish your heart.
Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.