< Psalms 25 >
1 A Psalme of David. Unto thee, O Lord, lift I vp my soule.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 My God, I trust in thee: let me not be confounded: let not mine enemies reioyce ouer mee.
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 So all that hope in thee, shall not be ashamed: but let them be confounded, that transgresse without cause.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Shew me thy waies, O Lord, and teache me thy paths.
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Leade me foorth in thy trueth, and teache me: for thou art the God of my saluation: in thee doe I trust all the day.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Remember, O Lord, thy tender mercies, and thy louing kindnesse: for they haue beene for euer.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Remember not the sinnes of my youth, nor my rebellions, but according to thy kindenesse remember thou me, euen for thy goodnesse sake, O Lord.
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Gracious and righteous is the Lord: therefore will he teache sinners in the way.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Them that be meeke, will hee guide in iudgement, and teach the humble his way.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 All the pathes of the Lord are mercie and trueth vnto such as keepe his couenant and his testimonies.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 For thy Names sake, O Lord, be merciful vnto mine iniquitie, for it is great.
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 What man is he that feareth the Lord? him wil he teache the way that hee shall chuse.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 His soule shall dwell at ease, and his seede shall inherite the land.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 The secrete of the Lord is reueiled to them, that feare him: and his couenant to giue them vnderstanding.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Mine eyes are euer towarde the Lord: for he will bring my feete out of the net.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Turne thy face vnto mee, and haue mercie vpon me: for I am desolate and poore.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 The sorowes of mine heart are enlarged: drawe me out of my troubles.
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Looke vpon mine affliction and my trauel, and forgiue all my sinnes.
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Beholde mine enemies, for they are manie, and they hate me with cruell hatred.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Keepe my soule, and deliuer me: let me not be confounded, for I trust in thee.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Let mine vprightnes and equitie preserue me: for mine hope is in thee.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Deliuer Israel, O God, out of all his troubles.
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!