< Psalms 24 >

1 A Psalme of David. The earth is the Lordes, and all that therein is: the worlde and they that dwell therein.
Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
2 For he hath founded it vpon the seas: and established it vpon the floods.
pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
3 Who shall ascende into the mountaine of the Lord? and who shall stand in his holy place?
Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
4 Euen he that hath innocent handes, and a pure heart: which hath not lift vp his minde vnto vanitie, nor sworne deceitfully.
Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
5 He shall receiue a blessing from the Lord, and righteousnesse from the God of his saluation.
Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
6 This is the generation of them that seeke him, of them that seeke thy face, this is Iaakob. (Selah)
Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
7 Lift vp your heads ye gates, and be ye lift vp ye euerlasting doores, and the King of glory shall come in.
Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
8 Who is this King of glorie? the Lord, strong and mightie, euen the Lord mightie in battell.
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
9 Lift vp your heads, ye gates, and lift vp your selues, ye euerlasting doores, and the King of glorie shall come in.
Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
10 Who is this King of glory? the Lord of hostes, he is the King of glorie. (Selah)
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)

< Psalms 24 >