< Psalms 19 >

1 To him that excelleth. A Psalme of Dauid. The heauens declare the glory of God, and the firmament sheweth ye worke of his hands.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
2 Day vnto day vttereth the same, and night vnto night teacheth knowledge.
Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
3 There is no speach nor language, where their voyce is not heard.
Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
4 Their line is gone forth through all the earth, and their words into the endes of the world: in them hath he set a tabernacle for the sunne.
Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
5 Which commeth forth as a bridegrome out of his chamber, and reioyceth like a mightie man to runne his race.
Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
6 His going out is from the ende of the heauen, and his compasse is vnto the endes of ye same, and none is hid from the heate thereof.
Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
7 The Lawe of the Lord is perfite, conuerting the soule: the testimonie of the Lord is sure, and giueth wisedome vnto the simple.
Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
8 The statutes of the Lord are right and reioyce the heart: the commandement of the Lord is pure, and giueth light vnto the eyes.
Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
9 The feare of the Lord is cleane, and indureth for euer: the iudgements of the Lord are trueth: they are righteous altogether,
Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
10 And more to be desired then golde, yea, then much fine golde: sweeter also then honie and the honie combe.
ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
11 Moreouer by them is thy seruant made circumspect, and in keeping of them there is great reward.
Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
12 Who can vnderstand his faultes? clense me from secret fautes.
Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
13 Keepe thy seruant also from presumptuous sinnes: let them not reigne ouer me: so shall I be vpright, and made cleane from much wickednes.
Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
14 Let the wordes of my mouth, and the meditation of mine heart be acceptable in thy sight, O Lord, my strength, and my redeemer.
Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.

< Psalms 19 >