< Psalms 147 >
1 Praise ye the Lord, for it is good to sing vnto our God: for it is a pleasant thing, and praise is comely.
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 The Lord doth builde vp Ierusalem, and gather together the dispersed of Israel.
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 He healeth those that are broken in heart, and bindeth vp their sores.
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
4 He counteth the nomber of the starres, and calleth them all by their names.
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Great is our Lord, and great is his power: his wisdome is infinite.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
6 The Lord relieueth the meeke, and abaseth the wicked to the ground.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Sing vnto the Lord with prayse: sing vpon the harpe vnto our God,
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 Which couereth the heauen with cloudes, and prepareth raine for the earth, and maketh the grasse to growe vpon the mountaines:
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 Which giueth to beasts their foode, and to the yong rauens that crie.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 He hath not pleasure in the strength of an horse, neither delighteth he in the legs of man.
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 But the Lord deliteth in them that feare him, and attende vpon his mercie.
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
12 Prayse the Lord, O Ierusalem: prayse thy God, O Zion.
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 For he hath made the barres of thy gates strong, and hath blessed thy children within thee.
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 He setteth peace in thy borders, and satisfieth thee with the floure of wheate.
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 He sendeth foorth his commandement vpon earth, and his worde runneth very swiftly.
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 He giueth snowe like wooll, and scattereth the hoare frost like ashes.
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 He casteth foorth his yce like morsels: who can abide the colde thereof?
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 He sendeth his worde and melteth them: he causeth his winde to blowe, and the waters flowe.
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 He sheweth his word vnto Iaakob, his statutes and his iudgements vnto Israel.
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 He hath not dealt so with euery nation, neither haue they knowen his iudgements. Prayse ye the Lord.
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.