< Psalms 144 >

1 A Psalme of David. Blessed be the Lord my strength, which teacheth mine hands to fight, and my fingers to battell.
Salimo la Davide. Atamandike Yehova Thanthwe langa, amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; zala zanga kumenya nkhondo.
2 He is my goodnes and my fortresse, my towre and my deliuerer, my shield, and in him I trust, which subdueth my people vnder me.
Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa, linga langa ndi mpulumutsi wanga, chishango changa mmene ine ndimathawiramo, amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.
3 Lord, what is man that thou regardest him! or the sonne of man that thou thinkest vpon him!
Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira, mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
4 Man is like to vanitie: his dayes are like a shadow, that vanisheth.
Munthu ali ngati mpweya; masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.
5 Bow thine heauens, O Lord, and come downe: touch the mountaines and they shall smoke.
Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi; khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
6 Cast forth the lightning and scatter them: shoote out thine arrowes, and consume them.
Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani; ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
7 Send thine hand from aboue: deliuer me, and take me out of the great waters, and from the hand of strangers,
Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba; landitseni ndi kundipulumutsa, ku madzi amphamvu, mʼmanja mwa anthu achilendo,
8 Whose mouth talketh vanitie, and their right hand is a right hand of falsehood.
amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
9 I wil sing a new song vnto thee, O God, and sing vnto thee vpon a viole, and an instrument of ten strings.
Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu; ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
10 It is he that giueth deliuerance vnto Kings, and rescueth Dauid his seruant from the hurtfull sworde.
kwa Iye amene amapambanitsa mafumu, amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.
11 Rescue me, and deliuer me from the hand of strangers, whose mouth talketh vanitie, and their right hand is a right hand of falshood:
Landitseni ndi kundipulumutsa, mʼmanja mwa anthu achilendo, amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
12 That our sonnes may be as the plantes growing vp in their youth, and our daughters as the corner stones, grauen after the similitude of a palace:
Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino, ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
13 That our corners may be full, and abounding with diuers sorts, and that our sheepe may bring forth thousands and ten thousand in our streetes:
Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza ndi zokolola za mtundu uliwonse. Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda pa mabusa athu.
14 That our oxen may be strong to labour: that there be none inuasion, nor going out, nor no crying in our streetes.
Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera. Sipadzakhala mingʼalu pa makoma, sipadzakhalanso kupita ku ukapolo, mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.
15 Blessed are the people, that be so, yea, blessed are the people, whose God is the Lord.
Odala anthu amene adzalandira madalitso awa; odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.

< Psalms 144 >