< Psalms 138 >

1 A Psalme of David. I will praise thee with my whole heart: euen before the gods will I praise thee.
Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
2 I will worship toward thine holy Temple and praise thy Name, because of thy louing kindenesse and for thy trueth: for thou hast magnified thy Name aboue all things by thy word.
Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
3 When I called, then thou heardest me, and hast encreased strength in my soule.
Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
4 All the Kings of the earth shall praise thee, O Lord: for they haue heard the wordes of thy mouth.
Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
5 And they shall sing of the wayes of the Lord, because the glory of the Lord is great.
Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
6 For the Lord is high: yet he beholdeth the lowly, but the proude he knoweth afarre off.
Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
7 Though I walke in the middes of trouble, yet wilt thou reuiue me: thou wilt stretch foorth thine hand vpon the wrath of mine enemies, and thy right hand shall saue me.
Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
8 The Lord will performe his worke toward me: O Lord, thy mercie endureth for euer: forsake not the workes of thine handes.
Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.

< Psalms 138 >