< Psalms 131 >
1 A song of degrees or Psalme of David. Lord, mine heart is not hautie, neither are mine eyes loftie, neither haue I walked in great matters and hid from me.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Davide. Inu Yehova, mtima wanga siwodzikuza, maso anga siwonyada; sinditengeteka mtima ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.
2 Surely I haue behaued my selfe, like one wained from his mother, and kept silence: I am in my selfe as one that is wained.
Koma moyo wanga ndawutontholetsa ndi kuwukhalitsa chete ngati mwana amene amayi ake amuletsa kuyamwa, moyo wanga mʼkati mwanga uli ngati mwana amene amuletsa kuyamwa.
3 Let Israel waite on the Lord from hencefoorth and for euer.
Yembekeza Yehova, iwe Israeli, kuyambira tsopano mpaka muyaya.