< Psalms 128 >

1 A song of degrees. Blessed is euery one that feareth the Lord and walketh in his wayes.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
2 When thou eatest the labours of thine hands, thou shalt be blessed, and it shall be well with thee.
Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
3 Thy wife shalbe as the fruitfull vine on the sides of thine house, and thy children like the oliue plantes round about thy table.
Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
4 Lo, surely thus shall the man be blessed, that feareth the Lord.
Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
5 The Lord out of Zion shall blesse thee, and thou shalt see the wealth of Ierusalem all the dayes of thy life.
Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
6 Yea, thou shalt see thy childrens children, and peace vpon Israel.
ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.

< Psalms 128 >