< Psalms 127 >
1 A song of degrees, or Psalme of Salomon. Except the Lord build the house, they labour in vaine that build it: except the Lord keepe the citie, the keeper watcheth in vaine.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
2 It is in vaine for you to rise earely, and to lie downe late, and eate the bread of sorow: but he wil surely giue rest to his beloued.
Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
3 Beholde, children are the inheritance of the Lord, and the fruite of the wombe his rewarde.
Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
4 As are the arrowes in the hand of ye strong man: so are the children of youth.
Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
5 Blessed is the man, that hath his quiuer full of them: for they shall not be ashamed, when they speake with their enemies in the gate.
Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.