< Psalms 126 >

1 A song of degrees, or Psalme of David. When ye Lord brought againe the captiuitie of Zion, we were like them that dreame.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
2 Then was our mouth filled with laughter, and our tongue with ioye: then sayd they among the heathen, The Lord hath done great things for them.
Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
3 The Lord hath done great things for vs, whereof we reioyce.
Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
4 O Lord, bring againe our captiuitie, as the riuers in the South.
Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
5 They that sowe in teares, shall reape in ioy.
Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
6 They went weeping and caried precious seede: but they shall returne with ioye and bring their sheaues.
Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.

< Psalms 126 >