< Psalms 124 >

1 A song of degrees, or Psalme of David. If the Lord had not bene on our side, (may Israel now say)
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, anene tsono Israeli,
2 If the Lord had not bene on our side, when men rose vp against vs,
akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, potiwukira anthuwo,
3 They had then swallowed vs vp quicke, when their wrath was kindled against vs.
iwo atatipsera mtima, akanatimeza amoyo;
4 Then the waters had drowned vs, and the streame had gone ouer our soule:
chigumula chikanatimiza, mtsinje ukanatikokolola,
5 Then had the swelling waters gone ouer our soule.
madzi a mkokomo akanatikokolola.
6 Praysed be the Lord, which hath not giuen vs as a praye vnto their teeth.
Atamandike Yehova, amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7 Our soule is escaped, euen as a bird out of the snare of the foulers: the snare is broken, and we are deliuered.
Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame yokodwa mu msampha wa mlenje; msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka.
8 Our helpe is in the Name of the Lord, which hath made heauen and earth.
Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

< Psalms 124 >