< Psalms 119 >

1 ALEPH. Blessed are those that are vpright in their way, and walke in the Lawe of the Lord.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Blessed are they that keepe his testimonies, and seeke him with their whole heart.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 Surely they woorke none iniquitie, but walke in his waies.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Thou hast commanded to keepe thy precepts diligently.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Oh that my waies were directed to keepe thy statutes!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Then should I not be confounded, when I haue respect vnto all thy commandements.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 I will praise thee with an vpright heart, when I shall learne the iudgements of thy righteousnesse.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 I will keepe thy statutes: forsake mee not ouerlong.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 BETH. Wherewith shall a yong man redresse his waie? in taking heede thereto according to thy woorde.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 With my whole heart haue I sought thee: let me not wander from thy commandements.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 I haue hid thy promise in mine heart, that I might not sinne against thee.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Blessed art thou, O Lord: teache mee thy statutes.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 With my lippes haue I declared all the iudgements of thy mouth.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 I haue had as great delight in the way of thy testimonies, as in all riches.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 I will meditate in thy precepts, and consider thy waies.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 I will delite in thy statutes, and I will not forget thy worde.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 GIMEL. Be beneficiall vnto thy seruant, that I may liue and keepe thy woorde.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Open mine eies, that I may see the wonders of thy Lawe.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 I am a stranger vpon earth: hide not thy commandements from me.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Mine heart breaketh for the desire to thy iudgements alway.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Thou hast destroied the proud: cursed are they that doe erre from thy commandements.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Remoue from mee shame and contempt: for I haue kept thy testimonies.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Princes also did sit, and speake against me: but thy seruant did meditate in thy statutes.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Also thy testimonies are my delite, and my counsellers.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 DALETH. My soule cleaueth to the dust: quicken me according to thy worde.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 I haue declared my waies, and thou heardest me: teache me thy statutes.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Make me to vnderstand ye way of thy precepts, and I will meditate in thy wondrous workes.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 My soule melteth for heauinesse: raise mee vp according vnto thy worde.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Take from mee the way of lying, and graunt me graciously thy Lawe.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 I haue chosen the way of trueth, and thy iudgements haue I laied before me.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 I haue cleaued to thy testimonies, O Lord: confound me not.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 I will runne the way of thy commandements, when thou shalt enlarge mine heart.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 HE. Teach mee, O Lord, the way of thy statutes, and I will keepe it vnto the ende.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Giue mee vnderstanding, and I will keepe thy Law: yea, I wil keepe it with my whole heart.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Direct mee in the path of thy commandements: for therein is my delite.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Incline mine heart vnto thy testimonies, and not to couetousnesse.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Turne away mine eies from regarding vanitie, and quicken me in thy way.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Stablish thy promise to thy seruaunt, because he feareth thee.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Take away my rebuke that I feare: for thy iudgements are good.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Beholde, I desire thy commandements: quicken me in thy righteousnesse,
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 VAV. And let thy louing kindnesse come vnto me, O Lord, and thy saluation according to thy promise.
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 So shall I make answere vnto my blasphemers: for I trust in thy woorde.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 And take not the woorde of trueth vtterly out of my mouth: for I waite for thy iudgements.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 So shall I alway keepe thy Lawe for euer and euer.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 And I will walke at libertie: for I seeke thy precepts.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 I will speake also of thy testimonies before Kings, and will not be ashamed.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 And my delite shalbe in thy commandements, which I haue loued.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Mine handes also will I lift vp vnto thy commandements, which I haue loued, and I will meditate in thy statutes.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 ZAIN. Remember the promise made to thy seruant, wherein thou hast caused me to trust.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 It is my comfort in my trouble: for thy promise hath quickened me.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 The proude haue had me exceedingly in derision: yet haue I not declined from thy Lawe.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 I remembred thy iudgements of olde, O Lord, and haue bene comforted.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Feare is come vpon mee for the wicked, that forsake thy Lawe.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Thy statutes haue beene my songes in the house of my pilgrimage.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 I haue remembred thy Name, O Lord, in the night, and haue kept thy Lawe.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 This I had because I kept thy precepts.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 CHETH. O Lord, that art my portion, I haue determined to keepe thy wordes.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 I made my supplication in thy presence with my whole heart: be mercifull vnto me according to thy promise.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 I haue considered my waies, and turned my feete into thy testimonies.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 I made haste and delaied not to keepe thy commandements.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 The bandes of the wicked haue robbed me: but I haue not forgotten thy Lawe.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 At midnight will I rise to giue thanks vnto thee, because of thy righteous iudgements.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 I am companion of all them that feare thee, and keepe thy precepts.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 The earth, O Lord, is full of thy mercie: teache me thy statutes.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 TETH. O Lord, thou hast delt graciously with thy seruant according vnto thy woorde.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Teach me good iudgement and knowledge: for I haue beleeued thy commandements.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Before I was afflicted, I went astray: but nowe I keepe thy woorde.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Thou art good and gracious: teach me thy statutes.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 The proud haue imagined a lie against me: but I wil keepe thy precepts with my whole heart.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Their heart is fatte as grease: but my delite is in thy Lawe.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 It is good for me that I haue beene afflicted, that I may learne thy statutes.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 The Lawe of thy mouth is better vnto me, then thousands of golde and siluer.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 IOD. Thine hands haue made me and fashioned me: giue mee vnderstanding therefore, that I may learne thy commandements.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 So they that feare thee, seeing mee shall reioyce, because I haue trusted in thy worde.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 I knowe, O Lord, that thy iudgements are right, and that thou hast afflicted me iustly.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 I pray thee that thy mercie may comfort me according to thy promise vnto thy seruant.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Let thy tender mercies come vnto me, that I may liue: for thy Lawe is my delite.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Let the proude be ashamed: for they haue dealt wickedly and falsely with me: but I meditate in thy precepts.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Let such as feare thee turne vnto me, and they that knowe thy testimonies.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Let mine heart bee vpright in thy statutes, that I be not ashamed.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 CAPH. My soule fainteth for thy saluation: yet I waite for thy worde.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Mine eyes faile for thy promise, saying, when wilt thou comfort me?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 For I am like a bottell in the smoke: yet doe I not forget thy statutes.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Howe many are the dayes of thy seruant? When wilt thou execute iudgement on them that persecute me?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 The proude haue digged pittes for mee, which is not after thy Lawe.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 All thy commandements are true: they persecute me falsely: helpe me.
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 They had almost consumed me vpon the earth: but I forsooke not thy precepts.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Quicken me according to thy louing kindnes: so shall I keepe the testimony of thy mouth.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 LAMED. O Lord, thy worde endureth for euer in heauen.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Thy trueth is from generation to generation: thou hast layed the foundation of the earth, and it abideth.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 They continue euen to this day by thine ordinances: for all are thy seruants.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Except thy Lawe had bene my delite, I should now haue perished in mine affliction.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 I wil neuer forget thy precepts: for by them thou hast quickened me.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 I am thine, saue me: for I haue sought thy precepts.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 The wicked haue waited for me to destroy me: but I will consider thy testimonies.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 I haue seene an ende of all perfection: but thy commandement is exceeding large.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 MEM. Oh howe loue I thy Lawe! it is my meditation continually.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 By thy commandements thou hast made mee wiser then mine enemies: for they are euer with mee.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 I haue had more vnderstading then all my teachers: for thy testimonies are my (meditation)
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 I vnderstoode more then the ancient, because I kept thy precepts.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 I haue refrained my feete from euery euil way, that I might keepe thy word.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 I haue not declined from thy iudgements: for thou didest teach me.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Howe sweete are thy promises vnto my mouth! yea, more then hony vnto my mouth.
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 By thy precepts I haue gotten vnderstanding: therefore I hate all the wayes of falshoode.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 NUN. Thy worde is a lanterne vnto my feete, and a light vnto my path.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 I haue sworne and will performe it, that I will keepe thy righteous iudgements.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 I am very sore afflicted: O Lord, quicken me according to thy word.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 O Lord, I beseeche thee accept the free offerings of my mouth, and teach mee thy iudgements.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 My soule is continually in mine hande: yet doe I not forget thy Lawe.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 The wicked haue layed a snare for mee: but I swarued not from thy precepts.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Thy testimonies haue I taken as an heritage for euer: for they are the ioy of mine heart.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 I haue applied mine heart to fulfill thy statutes alway, euen vnto the ende.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 SAMECH. I hate vaine inuentions: but thy Lawe doe I loue.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Thou art my refuge and shield, and I trust in thy worde.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Away from mee, yee wicked: for I will keepe the commandements of my God.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Stablish me according to thy promise, that I may liue, and disappoint me not of mine hope.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Stay thou mee, and I shall be safe, and I will delite continually in thy statutes.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Thou hast troden downe all them that depart from thy statutes: for their deceit is vaine.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Thou hast taken away all ye wicked of the earth like drosse: therefore I loue thy testimonies.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 My flesh trembleth for feare of thee, and I am afraide of thy iudgements.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 AIN. I haue executed iudgement and iustice: leaue me not to mine oppressours.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Answere for thy seruant in that, which is good, and let not the proude oppresse me.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Mine eyes haue failed in waiting for thy saluation, and for thy iust promise.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Deale with thy seruant according to thy mercie, and teache me thy statutes.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 I am thy seruant: graunt mee therefore vnderstanding, that I may knowe thy testimonies.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 It is time for thee Lord to worke: for they haue destroyed thy Lawe.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Therefore loue I thy commandements aboue golde, yea, aboue most fine golde.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Therefore I esteeme all thy precepts most iust, and hate all false wayes.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 PE. Thy testimonies are wonderfull: therefore doeth my soule keepe them.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 The entrance into thy wordes sheweth light, and giueth vnderstanding to the simple.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 I opened my mouth and panted, because I loued thy commandements.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Looke vpon mee and bee mercifull vnto me, as thou vsest to doe vnto those that loue thy Name.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Direct my steppes in thy worde, and let none iniquitie haue dominion ouer me.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Deliuer mee from the oppression of men, and I will keepe thy precepts.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Shew the light of thy countenance vpon thy seruant, and teache me thy statutes.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Mine eyes gush out with riuers of water, because they keepe not thy Lawe.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 TSADDI. Righteous art thou, O Lord, and iust are thy iudgements.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Thou hast commanded iustice by thy testimonies and trueth especially.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 My zeale hath euen consumed mee, because mine enemies haue forgotten thy wordes.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Thy word is prooued most pure, and thy seruant loueth it.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 I am small and despised: yet do I not forget thy precepts.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Thy righteousnesse is an euerlasting righteousnes, and thy Lawe is trueth.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Trouble and anguish are come vpon me: yet are thy commandements my delite.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 The righteousnes of thy testimonies is euerlasting: graunt me vnderstanding, and I shall liue.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 KOPH. I haue cried with my whole heart: heare me, O Lord, and I will keepe thy statutes.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 I called vpon thee: saue mee, and I will keepe thy testimonies.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 I preuented the morning light, and cried: for I waited on thy word.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Mine eyes preuent the night watches to meditate in thy word.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Heare my voyce according to thy louing kindenesse: O Lord, quicken me according to thy iudgement.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 They drawe neere, that follow after malice, and are farre from thy Lawe.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Thou art neere, O Lord: for all thy commandements are true.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 I haue knowen long since by thy testimonies, that thou hast established them for euer.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 RESH. Beholde mine affliction, and deliuer mee: for I haue not forgotten thy Lawe.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Pleade my cause, and deliuer me: quicken me according vnto thy word.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Saluation is farre from the wicked, because they seeke not thy statutes.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Great are thy tender mercies, O Lord: quicken me according to thy iudgements.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 My persecutours and mine oppressours are many: yet doe I not swarue from thy testimonies.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 I saw the transgressours and was grieued, because they kept not thy worde.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Consider, O Lord, how I loue thy preceptes: quicken mee according to thy louing kindenesse.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 The beginning of thy worde is trueth, and all the iudgements of thy righteousnesse endure for euer.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 SCHIN. Princes haue persecuted mee without cause, but mine heart stood in awe of thy wordes.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 I reioyce at thy worde, as one that findeth a great spoyle.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 I hate falshoode and abhorre it, but thy Lawe doe I loue.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Seuen times a day doe I praise thee, because of thy righteous iudgements.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 They that loue thy Law, shall haue great prosperitie, and they shall haue none hurt.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Lord, I haue trusted in thy saluation, and haue done thy commandements.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 My soule hath kept thy testimonies: for I loue them exceedingly.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 I haue kept thy precepts and thy testimonies: for all my wayes are before thee.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 TAV. Let my complaint come before thee, O Lord, and giue me vnderstanding, according vnto thy worde.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Let my supplication come before thee, and deliuer me according to thy promise.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 My lippes shall speake praise, when thou hast taught me thy statutes.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 My tongue shall intreate of thy word: for all thy commandements are righteous.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Let thine hand helpe me: for I haue chosen thy precepts.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 I haue longed for thy saluation, O Lord, and thy Lawe is my delite.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Let my soule liue, and it shall praise thee, and thy iudgements shall helpe me.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 I haue gone astraye like a lost sheepe: seeke thy seruant, for I doe not forget thy commandements.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalms 119 >