< Psalms 105 >

1 Praise the Lord, and call vpon his Name: declare his workes among the people.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Sing vnto him, sing prayse vnto him, and talke of all his wonderous workes.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Reioyce in his holy Name: let the heart of them that seeke the Lord, reioyce.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Seeke the Lord and his strength: seeke his face continually.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Remember his marueilous woorkes, that he hath done, his wonders and the iudgements of his mouth,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 Ye seede of Abraham his seruant, ye children of Iaakob, which are his elect.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 He is the Lord our God: his iudgements are through all the earth.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 He hath alway remembred his couenant and promise, that he made to a thousand generations,
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 Euen that which he made with Abraham, and his othe vnto Izhak:
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 And since hath confirmed it to Iaakob for a lawe, and to Israel for an euerlasting couenant,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 Saying, Vnto thee will I giue the land of Canaan, the lot of your inheritance.
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 Albeit they were fewe in nomber, yea, very fewe, and strangers in the land,
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 And walked about from nation to nation, from one kingdome to another people,
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 Yet suffered he no man to doe them wrong, but reprooued Kings for their sakes, saying,
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 Touche not mine anointed, and doe my Prophets no harme.
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Moreouer, he called a famine vpon ye land, and vtterly brake the staffe of bread.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 But he sent a man before them: Ioseph was solde for a slaue.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 They helde his feete in the stockes, and he was laide in yrons,
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 Vntill his appointed time came, and the counsell of the Lord had tryed him.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 The King sent and loosed him: euen the Ruler of the people deliuered him.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 He made him lord of his house, and ruler of all his substance,
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 That he shoulde binde his princes vnto his will, and teach his Ancients wisedome.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Then Israel came to Egypt, and Iaakob was a stranger in the land of Ham.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 And he increased his people exceedingly, and made them stronger then their oppressours.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 He turned their heart to hate his people, and to deale craftily with his seruants.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Then sent he Moses his seruant, and Aaron whom he had chosen.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 They shewed among them the message of his signes, and wonders in the land of Ham.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 He sent darkenesse, and made it darke: and they were not disobedient vnto his commission.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 He turned their waters into blood, and slewe their fish.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Their land brought foorth frogs, euen in their Kings chambers.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 He spake, and there came swarmes of flies and lice in all their quarters.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 He gaue them haile for raine, and flames of fire in their land.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 He smote their vines also and their figge trees, and brake downe the trees in their coastes.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 He spake, and the grashoppers came, and caterpillers innumerable,
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 And did eate vp all the grasse in their land, and deuoured the fruite of their ground.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 He smote also all the first borne in their land, euen the beginning of all their strength.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 He brought them forth also with siluer and golde, and there was none feeble among their tribes.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Egypt was glad at their departing: for the feare of them had fallen vpon them.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 He spred a cloude to be a couering, and fire to giue light in the night.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 They asked, and he brought quailes, and he filled them with the bread of heauen.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 He opened the rocke, and the waters flowed out, and ranne in the drye places like a riuer.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 For he remembred his holy promise to Abraham his seruant,
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 And he brought forth his people with ioy, and his chosen with gladnesse,
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 And gaue them the lands of the heathen, and they tooke the labours of the people in possession,
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 That they might keepe his statutes, and obserue his Lawes. Prayse ye the Lord.
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalms 105 >