< Psalms 104 >

1 My soule, prayse thou the Lord: O Lord my God, thou art exceeding great, thou art clothed with glorie and honour.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 Which couereth himselfe with light as with a garment, and spreadeth the heauens like a curtaine.
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 Which layeth the beames of his chambers in the waters, and maketh the cloudes his chariot, and walketh vpon the wings of the winde.
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 Which maketh his spirits his messengers, and a flaming fire his ministers.
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 He set the earth vpon her foundations, so that it shall neuer moue.
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 Thou coueredst it with the deepe as with a garment: the waters woulde stand aboue the mountaines.
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 But at thy rebuke they flee: at the voyce of thy thunder they haste away.
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 And the mountaines ascend, and the valleis descend to the place which thou hast established for them.
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 But thou hast set them a bounde, which they shall not passe: they shall not returne to couer the earth.
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 He sendeth the springs into the valleis, which runne betweene the mountaines.
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 They shall giue drinke to all the beasts of the fielde, and the wilde asses shall quench their thirst.
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 By these springs shall the foules of the heauen dwell, and sing among the branches.
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 He watereth the mountaines from his chambers, and the earth is filled with the fruite of thy workes.
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 He causeth grasse to growe for the cattell, and herbe for the vse of man, that he may bring forth bread out of the earth,
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 And wine that maketh glad the heart of man, and oyle to make the face to shine, and bread that strengtheneth mans heart.
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 The high trees are satisfied, euen the cedars of Lebanon, which he hath planted,
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 That ye birdes may make their nestes there: the storke dwelleth in the firre trees.
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 The high mountaines are for the goates: the rockes are a refuge for the conies.
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 He appoynted the moone for certaine seasons: the sunne knoweth his going downe.
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 Thou makest darkenesse, and it is night, wherein all the beastes of the forest creepe forth.
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 The lions roare after their praye, and seeke their meate at God.
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 When the sunne riseth, they retire, and couche in their dennes.
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 Then goeth man forth to his worke, and to his labour vntill the euening.
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 O Lord, howe manifolde are thy workes! in wisdome hast thou made them all: the earth is full of thy riches.
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 So is this sea great and wide: for therein are things creeping innumerable, both small beastes and great.
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 There goe the shippes, yea, that Liuiathan, whom thou hast made to play therein.
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 All these waite vpon thee, that thou maiest giue them foode in due season.
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 Thou giuest it to them, and they gather it: thou openest thine hand, and they are filled with good things.
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 But if thou hide thy face, they are troubled: if thou take away their breath, they dye and returne to their dust.
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 Againe if thou send forth thy spirit, they are created, and thou renuest the face of the earth.
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 Glory be to the Lord for euer: let the Lord reioyce in his workes.
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 He looketh on the earth and it trembleth: he toucheth the mountaines, and they smoke.
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 I will sing vnto the Lord all my life: I will prayse my God, while I liue.
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 Let my wordes be acceptable vnto him: I will reioyce in the Lord.
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 Let the sinners be consumed out of the earth, and the wicked till there be no more: O my soule, prayse thou the Lord. Prayse ye the Lord.
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.

< Psalms 104 >