< Psalms 103 >

1 A Psalme of David. My soule, prayse thou the Lord, and all that is within me, prayse his holy Name.
Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
2 My soule, prayse thou the Lord, and forget not all his benefites.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
3 Which forgiueth all thine iniquitie, and healeth all thine infirmities.
Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
4 Which redeemeth thy life from the graue, and crowneth thee with mercy and compassions.
amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
5 Which satisfieth thy mouth with good things: and thy youth is renued like the eagles.
amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
6 The Lord executeth righteousnes and iudgement to all that are oppressed.
Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
7 He made his wayes knowen vnto Moses, and his workes vnto the children of Israel.
Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
8 The Lord is full of compassion and mercie, slowe to anger and of great kindnesse.
Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
9 He will not alway chide, neither keepe his anger for euer.
Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
10 He hath not dealt with vs after our sinnes, nor rewarded vs according to our iniquities.
satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
11 For as high as the heauen is aboue ye earth, so great is his mercie toward them that feare him.
Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
12 As farre as the East is from the West: so farre hath he remooued our sinnes from vs.
monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
13 As a father hath compassion on his children, so hath the Lord compassion on them that feare him.
Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
14 For he knoweth whereof we be made: he remembreth that we are but dust.
pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
15 The dayes of man are as grasse: as a flowre of the fielde, so florisheth he.
Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
16 For the winde goeth ouer it, and it is gone, and the place thereof shall knowe it no more.
koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
17 But the louing kindnesse of the Lord endureth for euer and euer vpon them that feare him, and his righteousnes vpon childrens children,
Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
18 Vnto them that keepe his couenant, and thinke vpon his commandements to doe them.
iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
19 The Lord hath prepared his throne in heauen, and his Kingdome ruleth ouer all.
Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
20 Prayse the Lord, ye his Angels, that excell in strength, that doe his commandement in obeying the voyce of his worde.
Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
21 Prayse the Lord, all ye his hostes, ye his seruants that doe his pleasure.
Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
22 Prayse the Lord, all ye his workes, in all places of his dominion: my soule, prayse thou the Lord.
Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

< Psalms 103 >