< Proverbs 8 >
1 Doth not wisedome crie? and vnderstanding vtter her voyce?
Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
2 She standeth in the top of the high places by the way in the place of the paths.
Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
3 She cryeth besides the gates before the citie at the entrie of the doores,
Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
4 O men, I call vnto you, and vtter my voyce to the children of men.
Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
5 O ye foolish men, vnderstand wisedome, and ye, O fooles, be wise in heart.
Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Giue eare, for I will speake of excellent things, and the opening of my lippes, shall teache things that be right.
Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 For my mouth shall speake the trueth, and my lippes abhorre wickednesse.
Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 All the wordes of my mouth are righteous: there is no lewdenes, nor frowardnesse in them.
Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 They are all plaine to him that will vnderstande, and streight to them that woulde finde knowledge.
Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Receiue mine instruction, and not siluer, and knowledge rather then fine golde.
Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 For wisdome is better then precious stones: and all pleasures are not to be compared vnto her.
Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 I wisdome dwell with prudence, and I find foorth knowledge and counsels.
Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 The feare of the Lord is to hate euill as pride, and arrogancie, and the euill way: and a mouth that speaketh lewde things, I doe hate.
Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 I haue counsell and wisedome: I am vnderstanding, and I haue strength.
Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 By me, Kings reigne, and princes decree iustice.
Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 By me princes rule and the nobles, and all the iudges of the earth.
Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 I loue them that loue me: and they that seeke me earely, shall finde me.
Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 Riches and honour are with me: euen durable riches and righteousnesse.
Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 My fruite is better then golde, euen then fine golde, and my reuenues better then fine siluer.
Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 I cause to walke in the way of righteousnes, and in the middes of the paths of iudgement,
Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 That I may cause them that loue me, to inherite substance, and I will fill their treasures.
Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
22 The Lord hath possessed me in the beginning of his way: I was before his workes of olde.
“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
23 I was set vp from euerlasting, from the beginning and before the earth.
Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
24 When there were no depths, was I begotten, when there were no fountaines abounding with water.
Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
25 Before the mountaines were setled: and before the hilles, was I begotten.
Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
26 He had not yet made the earth, nor the open places, nor the height of the dust in the worlde.
lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
27 When hee prepared the heauens, I was there, when he set the compasse vpon the deepe.
Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
28 When he established the cloudes aboue, when he confirmed the fountaines of the deepe,
pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
29 When he gaue his decree to the Sea, that the waters shoulde not passe his commandement: when he appointed the foundations of the earth,
pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
30 Then was I with him as a nourisher, and I was dayly his delight reioycing alway before him,
Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
31 And tooke my solace in the compasse of his earth: and my delite is with the children of men.
Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
32 Therefore nowe hearken, O children, vnto me: for blessed are they that keepe my wayes.
“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
33 Heare instruction, and be ye wise, and refuse it not:
Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
34 blessed is the man that heareth mee, watching dayly at my gates, and giuing attendance at the postes of my doores.
Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
35 For he that findeth me, findeth life, and shall obteine fauour of the Lord.
Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
36 But he that sinneth against me, hurteth his owne soule: and all that hate me, loue death.
Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”