< Proverbs 6 >

1 My sonne, if thou be surety for thy neighbour, and hast striken hands with the stranger,
Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
2 Thou art snared with the wordes of thy mouth: thou art euen taken with the woordes of thine owne mouth.
ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
3 Doe this nowe, my sonne, and deliuer thy selfe: seeing thou art come into the hande of thy neighbour, goe, and humble thy selfe, and sollicite thy friends.
Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
4 Giue no sleepe to thine eyes, nor slumber to thine eyelids.
Usagone tulo, usawodzere.
5 Deliuer thy selfe as a doe from the hande of the hunter, and as a birde from the hande of the fouler.
Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
6 Goe to the pismire, O sluggarde: beholde her waies, and be wise.
Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 For shee hauing no guide, gouernour, nor ruler,
Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 Prepareth her meat in the sommer, and gathereth her foode in haruest.
komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 Howe long wilt thou sleepe, O sluggarde? when wilt thou arise out of thy sleepe?
Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 Yet a litle sleepe, a litle slumber, a litle folding of the hands to sleepe.
Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 Therefore thy pouertie commeth as one that trauaileth by the way, and thy necessitie like an armed man.
umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
12 The vnthriftie man and the wicked man walketh with a froward mouth.
Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
13 He maketh a signe with his eyes: he signifieth with his feete: he instructeth with his fingers.
amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
14 Lewde things are in his heart: he imagineth euill at all times, and raiseth vp contentions.
amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
15 Therefore shall his destruction come speedily: hee shall be destroyed suddenly without recouerie.
Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
16 These sixe things doeth the Lord hate: yea, his soule abhorreth seuen:
Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
17 The hautie eyes, a lying tongue, and the hands that shed innocent blood,
maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
18 An heart that imagineth wicked enterprises, feete that be swift in running to mischiefe,
mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
19 A false witnesse that speaketh lyes, and him that rayseth vp contentions among brethren.
mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
20 My sonne, keepe thy fathers commandement, and forsake not thy mothers instruction.
Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
21 Binde them alway vpon thine heart, and tye them about thy necke.
Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
22 It shall leade thee, when thou walkest: it shall watch for thee, when thou sleepest, and when thou wakest, it shall talke with thee.
Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
23 For the commandement is a lanterne, and instruction a light: and corrections for instruction are the way of life,
Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
24 To keepe thee from the wicked woman, and from ye flatterie of ye tongue of a strange woman.
kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
25 Desire not her beautie in thine heart, neither let her take thee with her eye lids.
Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
26 For because of the whorish woman a man is brought to a morsell of bread, and a woman wil hunt for the precious life of a man.
paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
27 Can a man take fire in his bosome, and his clothes not be burnt?
Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
28 Or can a man go vpon coales, and his feete not be burnt?
Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
29 So he that goeth in to his neighbours wife, shall not be innocent, whosoeuer toucheth her.
Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
30 Men do not despise a thiefe, when he stealeth, to satisfie his soule, because he is hungrie.
Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
31 But if he be founde, he shall restore seuen folde, or he shall giue all the substance of his house.
Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
32 But he that committeth adulterie with a woman, he is destitute of vnderstanding: he that doeth it, destroyeth his owne soule.
Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
33 He shall finde a wounde and dishonour, and his reproch shall neuer be put away.
Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
34 For ielousie is the rage of a man: therefore he will not spare in the day of vengeance.
Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
35 He cannot beare the sight of any raunsome: neither will he consent, though thou augment the giftes.
Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.

< Proverbs 6 >