< Proverbs 4 >

1 Heare, O ye children, the instruction of a father, and giue eare to learne vnderstanding.
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 For I doe giue you a good doctrine: therefore forsake yee not my lawe.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 For I was my fathers sonne, tender and deare in the sight of my mother,
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 When he taught me, and sayde vnto me, Let thine heart holde fast my woordes: keepe my commandements, and thou shalt liue.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Get wisedom: get vnderstading: forget not, neither decline from the woordes of my mouth.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Forsake her not, and shee shall keepe thee: loue her and shee shall preserue thee.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Wisedome is the beginning: get wisedome therefore: and aboue all thy possession get vnderstanding.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Exalt her, and she shall exalt thee: she shall bring thee to honour, if thou embrace her.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 She shall giue a comely ornamet vnto thine head, yea, she shall giue thee a crowne of glorie.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Heare, my sonne, and receiue my wordes, and the yeeres of thy life shalbe many.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 I haue taught thee in ye way of wisedom, and led thee in the pathes of righteousnesse.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Whe thou goest, thy gate shall not be strait, and when thou runnest, thou shalt not fall.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Take holde of instruction, and leaue not: keepe her, for shee is thy life.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Enter not into the way of the wicked, and walke not in the way of euill men.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Auoide it, and goe not by it: turne from it, and passe by.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 For they can not sleepe, except they haue done euill, and their sleepe departeth except they cause some to fall.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 For they eate the breade of wickednesse, and drinke the wine of violence.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 But the way of the righteous shineth as the light, that shineth more and more vnto the perfite day.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 The way of the wicked is as the darkenes: they knowe not wherein they shall fall.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 My sonne, hearken vnto my wordes, incline thine eare vnto my sayings.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Let them not depart from thine eyes, but keepe them in the middes of thine heart.
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 For they are life vnto those that find them, and health vnto all their flesh.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Keepe thine heart with all diligence: for thereout commeth life.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Put away from thee a froward mouth, and put wicked lippes farre from thee.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Let thine eyes beholde the right, and let thine eyelids direct thy way before thee.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Ponder the path of thy feete, and let all thy waies be ordred aright.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Turne not to the right hande, nor to the left, but remooue thy foote from euill.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Proverbs 4 >