< Proverbs 31 >

1 THE WORDS OF KING LEMUEL: The prophecie which his mother taught him.
Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 What my sonne! and what ye sonne of my wombe! and what, O sonne of my desires!
Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 Giue not thy strength vnto women, nor thy wayes, which is to destroy Kings.
Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 It is not for Kings, O Lemuel, it is not for Kings to drink wine nor for princes strog drinke,
Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 Lest he drinke and forget the decree, and change the iudgement of all the children of affliction.
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 Giue ye strong drinke vnto him that is readie to perish, and wine vnto them that haue griefe of heart.
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 Let him drinke, that he may forget his pouertie, and remember his miserie no more.
amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 Open thy mouth for the domme in the cause of all the children of destruction.
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 Open thy mouth: iudge righteously, and iudge the afflicted, and the poore.
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
10 Who shall finde a vertuous woman? for her price is farre aboue the pearles.
Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 The heart of her husband trusteth in her, and he shall haue no neede of spoyle.
Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 She will doe him good, and not euill all the dayes of her life.
Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 She seeketh wooll and flaxe, and laboureth cheerefully with her handes.
Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 She is like the shippes of marchants: shee bringeth her foode from afarre.
Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
15 And she riseth, whiles it is yet night: and giueth the portion to her houshold, and the ordinarie to her maides.
Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 She considereth a field, and getteth it: and with the fruite of her handes she planteth a vineyarde.
Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 She girdeth her loynes with strength, and strengtheneth her armes.
Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 She feeleth that her marchandise is good: her candle is not put out by night.
Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 She putteth her handes to the wherue, and her handes handle the spindle.
Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 She stretcheth out her hand to the poore, and putteth foorth her hands to the needie.
Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 She feareth not the snowe for her familie: for all her familie is clothed with skarlet.
Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 She maketh her selfe carpets: fine linen and purple is her garment.
Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 Her husband is knowen in the gates, when he sitteth with the Elders of the land.
Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 She maketh sheetes, and selleth them, and giueth girdels vnto the marchant.
Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 Strength and honour is her clothing, and in the latter day she shall reioyce.
Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 She openeth her mouth with wisdome, and the lawe of grace is in her tongue.
Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 She ouerseeth the wayes of her housholde, and eateth not the bread of ydlenes.
Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 Her children rise vp, and call her blessed: her husband also shall prayse her, saying,
Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 Many daughters haue done vertuously: but thou surmountest them all.
“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
30 Fauour is deceitfull, and beautie is vanitie: but a woman that feareth the Lord, she shall be praysed.
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 Giue her of the fruite of her hands, and let her owne workes prayse her in the gates.
Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.

< Proverbs 31 >