< Proverbs 27 >
1 Boast not thy selfe of to morowe: for thou knowest not what a day may bring forth.
Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
2 Let another man prayse thee, and not thine owne mouth: a stranger, and not thine owne lips.
Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
3 A stone is heauie, and the sand weightie: but a fooles wrath is heauier then them both.
Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
4 Anger is cruell, and wrath is raging: but who can stand before enuie?
Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
5 Open rebuke is better then secret loue.
Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
6 The wounds of a louer are faithful, and the kisses of an enemie are pleasant.
Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
7 The person that is full, despiseth an hony combe: but vnto the hungry soule euery bitter thing is sweete.
Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
8 As a bird that wandreth from her nest, so is a man that wandreth from his owne place.
Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
9 As oyntment and perfume reioyce the heart, so doeth the sweetenes of a mans friend by hearty counsell.
Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
10 Thine owne friend and thy fathers friend forsake thou not: neither enter into thy brothers house in the day of thy calamitie: for better is a neighbour that is neere, then a brother farre off.
Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
11 My sonne, be wise, and reioyce mine heart, that I may answere him that reprocheth me.
Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
12 A prudent man seeth the plague, and hideth himselfe: but the foolish goe on still, and are punished.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
13 Take his garment that is surety for a stranger, and a pledge of him for the stranger.
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
14 He that prayseth his friend with a loude voyce, rising earely in the morning, it shall be counted to him as a curse.
Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
15 A continual dropping in the day of raine, and a contentious woman are alike.
Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
16 He that hideth her, hideth the winde, and she is as ye oyle in his right hand, that vttereth it selfe.
Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
17 Yron sharpeneth yron, so doeth man sharpen the face of his friend.
Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
18 He that keepeth the fig tree, shall eate the fruite thereof: so he that waiteth vpon his master, shall come to honour.
Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
19 As in water face answereth to face, so the heart of man to man.
Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
20 The graue and destruction can neuer be full, so the eyes of man can neuer be satisfied. (Sheol )
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol )
21 As is the fining pot for siluer and the fornace for golde, so is euery man according to his dignitie.
Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
22 Though thou shouldest bray a foole in a morter among wheate brayed with a pestell, yet will not his foolishnes depart from him.
Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
23 Be diligent to know ye state of thy flocke, and take heede to the heardes.
Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
24 For riches remaine not alway, nor the crowne from generation to generation.
Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
25 The hey discouereth it selfe, and the grasse appeareth, and the herbes of the mountaines are gathered.
Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
26 The lambes are for thy clothing, and the goates are the price of the fielde.
ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
27 And let the milke of the goates be sufficient for thy foode, for the foode of thy familie, and for the sustenance of thy maydes.
Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.