< Proverbs 22 >

1 A good name is to be chosen aboue great riches, and louing fauour is aboue siluer and aboue golde.
Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
2 The rich and poore meete together: the Lord is the maker of them all.
Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
3 A prudent man seeth the plague, and hideth himselfe: but the foolish goe on still, and are punished.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
4 The rewarde of humilitie, and the feare of God is riches, and glory, and life.
Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
5 Thornes and snares are in the way of the frowarde: but he that regardeth his soule, will depart farre from them.
Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
6 Teache a childe in the trade of his way, and when he is olde, he shall not depart from it.
Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
7 The rich ruleth the poore, and the borower is seruant to the man that lendeth.
Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
8 He that soweth iniquitie, shall reape affliction, and the rodde of his anger shall faile.
Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
9 He that hath a good eye, he shalbe blessed: for he giueth of his bread vnto the poore.
Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
10 Cast out the scorner, and strife shall go out: so contention and reproche shall cease.
Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
11 Hee that loueth purenesse of heart for the grace of his lippes, the King shalbe his friend.
Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
12 The eyes of the Lord preserue knowledge: but hee ouerthroweth the wordes of the transgressour.
Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
13 The slouthfull man saith, A lyon is without, I shall be slaine in the streete.
Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
14 The mouth of strage women is as a deepe pit: he with whom the Lord is angry, shall fall therein.
Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
15 Foolishnesse is bounde in the heart of a childe: but the rodde of correction shall driue it away from him.
Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
16 Hee that oppresseth the poore to increase him selfe, and giueth vnto the riche, shall surely come to pouertie.
Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
17 Incline thine eare, and heare the wordes of the wise, and apply thine heart vnto my knowledge.
Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
18 For it shalbe pleasant, if thou keepe them in thy bellie, and if they be directed together in thy lippes.
Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
19 That thy confidence may be in the Lord, I haue shewed thee this day: thou therefore take heede.
Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
20 Haue not I written vnto thee three times in counsels and knowledge,
Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
21 That I might shewe thee the assurance of the wordes of trueth to answere the wordes of trueth to them that sende to thee?
malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
22 Robbe not the poore, because hee is poore, neither oppresse the afflicted in iudgement.
Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
23 For the Lord will defende their cause, and spoyle the soule of those that spoyle them.
pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
24 Make no friendship with an angrie man, neither goe with the furious man,
Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
25 Least thou learne his wayes, and receiue destruction to thy soule.
kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
26 Be not thou of them that touch the hand, nor among them that are suretie for debts.
Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
27 If thou hast nothing to paye, why causest thou that he should take thy bed from vnder thee?
ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
28 Thou shalt not remooue the ancient bounds which thy fathers haue made.
Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
29 Thou seest that a diligent man in his businesse standeth before Kings, and standeth not before the base sort.
Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.

< Proverbs 22 >