< Proverbs 2 >

1 My sonne, if thou wilt receiue my wordes, and hide my commandements within thee,
Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2 And cause thine eares to hearken vnto wisdome, and encline thine heart to vnderstanding,
ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3 (For if thou callest after knowledge, and cryest for vnderstanding:
ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4 If thou seekest her as siluer, and searchest for her as for treasures,
ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5 Then shalt thou vnderstand the feare of the Lord, and finde the knowledge of God.
ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
6 For the Lord giueth wisdome, out of his mouth commeth knowledge and vnderstanding.
Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
7 He preserueth the state of the righteous: he is a shielde to them that walke vprightly,
Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
8 That they may keepe the wayes of iudgement: and he preserueth the way of his Saintes)
pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
9 Then shalt thou vnderstand righteousnes, and iudgement, and equitie, and euery good path.
Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10 When wisdome entreth into thine heart, and knowledge deliteth thy soule,
Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11 Then shall counsell preserue thee, and vnderstanding shall keepe thee,
Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
12 And deliuer thee from the euill way, and from the man that speaketh froward things,
Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
13 And from them that leaue the wayes of righteousnes to walke in the wayes of darkenes:
amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
14 Which reioyce in doing euill, and delite in the frowardnesse of the wicked,
amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15 Whose wayes are crooked and they are lewde in their paths.
Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
16 And it shall deliuer thee from the strange woman, euen from the stranger, which flattereth with her wordes.
Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17 Which forsaketh the guide of her youth, and forgetteth the couenant of her God.
amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18 Surely her house tendeth to death, and her paths vnto the dead.
Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
19 All they that goe vnto her, returne not againe, neither take they holde of the wayes of life.
Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
20 Therefore walke thou in the way of good men, and keepe the wayes of the righteous.
Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21 For the iust shall dwell in the land, and the vpright men shall remaine in it.
Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22 But the wicked shalbe cut off from ye earth, and the transgressours shalbe rooted out of it.
Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

< Proverbs 2 >