< Proverbs 16 >
1 The preparations of the heart are in man: but the answere of the tongue is of the Lord.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 All the wayes of a man are cleane in his owne eyes: but the Lord pondereth the spirits.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Commit thy workes vnto the Lord, and thy thoughts shalbe directed.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 The Lord hath made all things for his owne sake: yea, euen the wicked for the day of euill.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 All that are proude in heart, are an abomination to the Lord: though hand ioyne in hand, he shall not be vnpunished.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 By mercy and trueth iniquitie shalbe forgiuen, and by the feare of the Lord they depart from euill.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 When the wayes of a man please the Lord, he will make also his enemies at peace with him.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Better is a litle with righteousnesse, then great reuenues without equitie.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 The heart of man purposeth his way: but the Lord doeth direct his steppes.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 A diuine sentence shalbe in the lips of the King: his mouth shall not transgresse in iudgement.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 A true weight and balance are of the Lord: all the weightes of the bagge are his worke.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 It is an abomination to Kings to commit wickednes: for the throne is stablished by iustice.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Righteous lips are the delite of Kings, and the King loueth him that speaketh right things.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 The wrath of a King is as messengers of death: but a wise man will pacifie it.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 In the light of the Kings coutenance is life: and his fauour is as a cloude of the latter raine.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 Howe much better is it to get wisedome then golde? and to get vnderstanding, is more to be desired then siluer.
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 The pathe of the righteous is to decline from euil, and hee keepeth his soule, that keepeth his way.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Pride goeth before destruction, and an high minde before the fall.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Better it is to be of humble minde with the lowly, then to deuide the spoyles with the proude.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 He that is wise in his busines, shall finde good: and he that trusteth in the Lord, he is blessed.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 The wise in heart shall bee called prudent: and the sweetenesse of the lippes shall increase doctrine.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Vnderstading is welspring of life vnto them that haue it: and the instruction of fooles is folly.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 The heart of the wise guideth his mouth wisely, and addeth doctrine to his lippes.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Faire wordes are as an hony combe, sweetenesse to the soule, and health to the bones.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 There is a way that seemeth right vnto man: but the issue thereof are the wayes of death.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 The person that traueileth, traueileth for himselfe: for his mouth craueth it of him.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 A wicked man diggeth vp euill, and in his lippes is like burning fire.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 A frowarde person soweth strife: and a tale teller maketh diuision among princes.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 A wicked man deceiueth his neighbour, and leadeth him into the way that is not good.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 He shutteth his eyes to deuise wickednes: he moueth his lippes, and bringeth euil to passe.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 Age is a crowne of glory, when it is founde in the way of righteousnes.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 He that is slowe vnto anger, is better then the mightie man: and hee that ruleth his owne minde, is better then he that winneth a citie.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 The lot is cast into the lap: but the whole disposition thereof is of the Lord.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.