< Numbers 6 >

1 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Speake vnto the children of Israel, and say vnto them, When a man or a woman doeth separate themselues to vowe a vowe of a Nazarite to separate himselfe vnto the Lord,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri,
3 He shall abstaine from wine and strong drinke, and shall drinke no sowre wine nor sowre drinke, nor shall drinke any licour of grapes, neither shall eate fresh grapes nor dryed.
sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma.
4 As long as his abstinence endureth, shall hee eat nothing that is made of the wine of the vine, neither the kernels, nor the huske.
Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’
5 While hee is separate by his vowe, the rasor shall not come vpon his head, vntill the dayes be out, in the which he separateth him selfe vnto the Lord, he shalbe holy, and shall let the lockes of the heare of his head growe.
“‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’
6 During the time that he separateth himselfe vnto the Lord, he shall come at no dead body:
Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo.
7 Hee shall not make himselfe vncleane at the death of his father, or mother, brother, or sister: for the consecration of his God is vpon his head.
Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake.
8 All the dayes of his separation he shalbe holy to the Lord.
Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.
9 And if any dye suddenly by him, or hee beware, then the head of his consecration shall be defiled, and he shall shaue his head in the day of his clensing: in the seuenth day he shall shaue it.
“Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri.
10 And in the eight day hee shall bring two turtles, or two yong pigeons to the Priest, at the doore of the Tabernacle of the Congregation.
Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano.
11 Then the Priest shall prepare the one for a sinne offering, and the other for a burnt offering, and shall make an atonement for him, because he sinned by the dead: so shall he halowe his head the same day,
Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake.
12 And he shall consecrate vnto the Lord the dayes of his separation, and shall bring a lambe of a yeere olde for a trespasse offering, and the first dayes shalbe voide: for his consecration was defiled.
Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.
13 This then is the lawe of the Nazarite: When the time of his consecration is out, he shall come to the doore of the Tabernacle of the Congregation,
“Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
14 And hee shall bring his offering vnto the Lord, an hee lambe of a yeere olde without blemish for a burnt offering, and a shee lambe of a yere olde without blemish for a sinne offring, and a ramme without blemish for peace offrings,
Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano,
15 And a basket of vnleauened bread, of cakes of fine floure, mingled with oyle, and wafers of vnleauened bread anointed with oile, with their meate offring, and their drinke offrings:
ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.
16 The which the Priest shall bring before the Lord, and make his sinne offering and his burnt offering.
“Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza.
17 He shall prepare also the ram for a peace offring vnto the Lord, with the basket of vnleauened bread, and the Priest shall make his meate offring, and his drinke offring.
Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.
18 And the Nazarite shall shaue the head of his consecration at the doore of the Tabernacle of the Congregation, and shall take the heare of the head of his consecration, and put it in the fire, which is vnder the peace offring.
“Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.
19 Then the Priest shall take ye sodden shoulder of the ramme, and an vnleauened cake out of the basket, and a wafer vnleauened, and put them vpon the hands of the Nazarite, after he hath shauen his consecration.
“Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija.
20 And the Priest shall shake them to and from before the Lord: this is an holy thing for the Priest besides the shaken breast, and besides the heaue shoulder: so afterwarde the Nazarite may drinke wine.
Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.
21 This is the Lawe of the Nazarite, which he hath vowed, and of his offering vnto the Lord for his consecration, besides that that hee is able to bring: according to the vowe which he vowed, so shall he do after the lawe of his consecration.
“Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”
22 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
23 Speake vnto Aaron and to his sonnes, saying, Thus shall ye blesse the childre of Israel, and say vnto them,
“Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,
24 The Lord blesse thee, and keepe thee,
“‘Yehova akudalitse ndi kukusunga;
25 The Lord make his face shine vpon thee, and be merciful vnto thee,
Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;
26 The Lord lift vp his coutenance vpon thee, and giue thee peace.
Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.’”
27 So they shall put my Name vpon the children of Israel, and I wil blesse them.
Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.

< Numbers 6 >