< Numbers 36 >

1 Then the chiefe fathers of the familie of the sonnes of Gilead, the sonne of Machir, the sonne of Manasseh, of the families of the sones of Ioseph, came, and spake before Moses, and before the princes, the chiefe fathers of the children of Israel,
Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
2 And saide, The Lord commanded my lord to giue the land to inherit by lot to the children of Israel: and my lord was commanded by the Lord, to giue the inheritance of Zelophehad our brother vnto his daughters.
Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
3 If they bee married to any of the sonnes of the other tribes of the children of Israel, then shall their inheritance be taken away from the inheritance of our fathers, and shalbe put vnto the inheritance of the tribe whereof they shalbe: so shall it be taken away from the lot of our inheritance.
Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
4 Also when the Iubile of the children of Israel commeth, then shall their inheritance be put vnto the inheritance of the tribe whereof they shall be: so shall their inheritance be taken away from the inheritance of the tribe of our fathers.
Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
5 Then Moses commanded the children of Israel, according to the word of the Lord, saying, The tribe of the sonnes of Ioseph haue said well.
Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
6 This is the thing that the Lord hath commanded, concerning the daughters of Zelophehad, saying, They shall be wiues, to whome they thinke best, onely to the familie of the tribe of their father shall they marry:
Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
7 So shall not the inheritance of the children of Israel remoue from tribe to tribe, for euery one of the children of Israel shall ioyne himselfe to the inheritance of the tribe of his fathers.
kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
8 And euery daughter that possesseth any inheritance of the tribes of the children of Israel, shalbe wife vnto one of the familie of the tribe of her father: that the children of Israel may enioye euery man the inheritance of their fathers.
Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
9 Neither shall the inheritance go about from tribe to tribe: but euery one of the tribes of the childre of Israel shall sticke to his own inheritace.
Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
10 As the Lord commanded Moses, so did the daughters of Zelophehad.
Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
11 For Mahlah, Tirzah, and Hoglah, and Milcah, and Noah the daughters of Zelophehad were married vnto their fathers brothers sonnes,
Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
12 They were wiues to certaine of the families of the sonnes of Manasseh the sonne of Ioseph: so their inheritance remained in the tribe of the familie of their father.
Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
13 These are the commandements and lawes which the Lord commanded by the hand of Moses, vnto the children of Israel in the plaine of Moab, by Iorden toward Iericho.
Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.

< Numbers 36 >