< Numbers 32 >
1 Nowe the children of Reuben, and the children of Gad had an exceeding great multitude of cattell: and they sawe the lande of Iazer, and the lande of Gilead, that it was an apt place for cattel.
Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo.
2 Then the children of Gad, and the childre of Reuben came, and spake vnto Moses and to Eleazar the Priest, and vnto the princes of the Congregation, saying,
Choncho Arubeni ndi Agadi anapita kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa atsogoleri a anthu ndi kunena kuti,
3 The land of Ataroth, and Dibon, and Iazer, and Nimrah, and Heshbon, and Elealeh, and Shebam, and Nebo, and Beon,
“Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni,
4 Which countrey the Lord smote before the Congregation of Israel, is a lande meete for cattell, and thy seruants haue cattell:
dziko lomwe Yehova anagonjetsa pamaso pa Aisraeli, ndiwo malo woyenera ziweto, ndipo atumiki anufe tili ndi ziweto.
5 Wherefore, said they, if we haue foud grace in thy sight, let this lande be giuen vnto thy seruants for a possession, and bring vs not ouer Iorde.
Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’”
6 And Moses said vnto the children of Gad, and to the children of Reuben, Shall your brethren goe to warre, and ye tary heere?
Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno?
7 Wherefore now discourage ye the heart of the children of Israel, to goe ouer into the lande, which the Lord hath giuen them?
Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa?
8 Thus did your fathers when I sent them from Kadesh-barnea to see the lande.
Izi ndi zimene makolo anu anachita pamene ndinawatuma kuchokera ku Kadesi kukaona dzikolo.
9 For when they went vp euen vnto the riuer of Eshcol, and sawe the land: they discouraged the heart of the childre of Israel, that they woulde not goe into the lande, which the Lord had giuen them.
Atapita ku chigwa cha Esikolo, ndi kuliona dzikolo, anafowoketsa Aisraeli kuti asalowe mʼdziko limene Yehova anawapatsa.
10 And the Lordes wrath was kindled the same day, and he did sweare, saying,
Yehova anakwiya tsiku limenelo ndipo analumbira kuti,
11 None of the men that came out of Egypt from twentie yeere olde and aboue, shall see the land for the which I sware vnto Abraham, to Izhak, and to Iaakob, because they haue not wholly followed me:
‘Chifukwa sananditsatire ndi mtima wonse, palibe ndi mmodzi yemwe mwa amuna a zaka makumi awiri kapena kuposa pamenepo, amene anachokera ku Igupto, amene adzaone dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
12 Except Caleb the sonne of Iephunneh the Kenesite, and Ioshua the sonne of Nun: for they haue constantly followed the Lord.
Palibe ndi mmodzi yemwe kupatula Kalebe mwana wa Yefune, Mkeni, ndi Yoswa mwana wa Nuni chifukwa anatsatira Yehova ndi mtima wonse.’
13 And the Lord was very angry with Israel, and made them wander in the wildernesse fourty yeeres, vntill all the generation that had done euill in the sight of the Lord were consumed.
Yehova anakwiyira Aisraeli kwambiri ndipo anawachititsa kuyenda mʼchipululu zaka makumi anayi, mpaka mʼbado wonse wa anthu amene anachita choyipa pamaso pake unatha.
14 And behold, ye are risen vp in your fathers steade as an encrease of sinfull men, still to augment the fierce wrath of the Lord, toward Israel.
“Ndipo onani tsopano, inu mʼbado wochimwa, mwalowa mʼmalo mwa makolo anu ndipo mwachititsa kuti Yehova akwiyire Israeli kwambiri.
15 For if ye turne away from following him, he will yet againe leaue the people in the wildernesse, and ye shall destroy all this folke.
Ngati muleka kumutsata, Iye adzawasiyiranso anthu onsewa mʼchipululu ndipo mudzawonongetsa anthu onsewa.”
16 And they went neere to him, and said, We will builde sheepe foldes here for our sheepe, and for our cattell, and cities for our children.
Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu.
17 But we our selues will be readie armed to go before the children of Israel, vntill we haue brought them vnto their place: but our childre shall dwell in the defenced cities, because of the inhabitants of the lande.
Koma ndife okonzeka kutenga zida za nkhondo ndi kupita pamodzi ndi Aisraeli mpaka titakawafikitsa ku malo awo. Panopa, akazi ndi ana athu akhala mʼmizinda yotetezedwa, kuwateteza kwa anthu okhala mʼdzikoli.
18 We will not returne vnto our houses, vntil the children of Israel haue inherited, euery man his inheritance.
Sitidzabwerera ku midzi yathu mpaka Mwisraeli aliyense atalandira cholowa chake.
19 Neither wil we inherite with them beyond Iorden and on that side, because our inheritance is fallen to vs on this side Iorden Eastwarde.
Sitidzalandira cholowa chilichonse pamodzi nawo ku tsidya lina la Yorodani, chifukwa cholowa chathu tachipezera ku tsidya lino la kummawa kwa Yorodani.”
20 And Moses saide vnto them, If ye will doe this thing, and goe armed before the Lord to warre:
Tsono Mose anati kwa anthuwo, “Ngati inu mudzachita zimenezi, kutenga zida zankhondo pamaso pa Yehova kuti muchite nkhondo,
21 And will goe euery one of you in harnesse ouer Iorden before the Lord, vntill he hath cast out his enemies from his sight:
ndipo ngati nonsenu mudzapita ndi zida kuwoloka Yorodani pamaso pa Yehova mpaka atachotsa adani ake pamaso pake,
22 And vntill the land be subdued before the Lord, then ye shall returne and be innocent toward the Lord, and toward Israel: and this land shalbe your possession before the Lord.
dzikolo nʼkugonja pamaso pa Yehova, mudzabwera ndi kukhala mfulu pamaso pa Yehova ndi Aisraeli. Ndipo dziko lino lidzakhala lanu pamaso pa Yehova.
23 But if ye will not doe so, beholde, ye haue sinned against the Lord, and be sure, that your sinne will finde you out.
“Koma mukalephera kuchita izi, mudzakhala mukuchimwira Yehova. Ndipo dziwani kuti tchimo lanu lidzakupezani.
24 Builde you then cities for your children and folds for your sheepe, and do that ye haue spoke.
Amangireni akazi ndi ana anu mizinda, mangani makola a ziweto zanu, koma chitani zomwe mwalonjeza.”
25 Then the children of Gad and the children of Reuben spake vnto Moses, saying, Thy seruats will doe as my lorde commandeth:
Agadi ndi Arubeni anati kwa Mose, “Ife antchito anu tidzachita monga mbuye wathu mwalamulira.
26 Our childre, our wiues, our sheepe, and al our cattell shall remaine there in the cities of Gilead,
Ana ndi akazi athu, ziweto zathu zina ndi ngʼombe zidzatsala kuno ku mizinda ya Giliyadi,
27 But thy seruants will goe euery one armed to warre before the Lord for to fight, as my lorde saith.
koma antchito anufe, mwamuna aliyense amene ali ndi chida cha nkhondo, adzawoloka kukamenya nkhondo pamaso pa Yehova monga mbuye wathu wanenera.”
28 So concerning them, Moses commanded Eleazar the Priest, and Ioshua the sonne of Nun, and the chiefe fathers of the tribes of the children of Israel:
Choncho Mose anapereka malamulo awa kwa wansembe Eliezara, kwa Yoswa mwana wa Nuni ndi kwa akulu a mafuko a Aisraeli.
29 And Moses said vnto them, If the children of Gad, and the children of Reuben, will go with you ouer Iorden, all armed to fight before the Lord, then when the land is subdued before you, ye shall giue the the lad of Gilead for a possessio:
Mose anawawuza kuti, ngati Agadi ndi Arubeni, mwamuna aliyense wokonzekera nkhondo, awoloka Yorodani pamodzi ndi inu pamaso pa Yehova, ndipo dzikolo nʼkugonjetsedwa pamaso panu, mudzawapatse dziko la Giliyadi kukhala lawo.
30 But if they will not goe ouer with you armed, then they shall haue their possessions amog you in the land of Canaan.
Koma ngati sawoloka pamodzi nanu ndi zida zankhondo, ayenera kulandira cholowa chawo pamodzi ndi inu ku Kanaani.
31 And the children of Gad, and the children of Reuben answered, saying, As the Lord hath said vnto thy seruants, so will we doe.
Agadi ndi Arubeni anayankha kuti, “Antchito anu adzachita zimene Yehova wanena.
32 We will goe armed before the Lord into the lande of Canaan: that the possession of our inheritance may be to vs on this side Iorden.
Tidzawoloka pamaso pa Yehova ndipo tidzalowa mu Kanaani ndi zida zankhondo, koma cholowa chathu chidzakhala ku tsidya lino la Yorodani.”
33 So Moses gaue vnto them, euen to the children of Gad, and to the children of Reuben, and to halfe the tribe of Manasseh the sonne of Ioseph, the kingdome of Sihon King of the Amorites, and the kingdome of Og King of Bashan, the lande with the cities thereof and coastes, euen the cities of the countrey round about.
Choncho Mose anapatsa Agadi, Arubeni ndi theka la fuko la Manase mwana wa Yosefe dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi, mfumu ya ku Basani, dziko lonse, mizinda yake ndi midzi yowazungulira.
34 Then the children of Gad built Dibon, and Ataroth, and Aroer,
Agadi anamanga Diboni, Ataroti, Aroeri,
35 And Atroth, Shophan, and Iazer, and Iogbehah,
Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha,
36 And Beth-nimrah, and Beth-haran, defenced cities: also sheepe foldes.
Beti-Nimira ndi Beti-Harani mizinda ya malinga. Anamanganso makola a ziweto zawo.
37 And the children of Reuben built Heshbon, and Elealeh, and Kiriathaim,
Ndipo Arubeni anamanga Hesiboni, Eleali, Kiriataimu,
38 And Nebo, and Baal-meon, and turned their names, and Shibmah: and gaue other names vnto the cities which they built.
Nebo ndi Baala-Meoni (mayina awa anasinthidwa) ndi Sibima. Anapereka mayina ku mizinda ina yomwe anamangayo.
39 And the children of Machir the sonne of Manasseh went to Gilead, and tooke it, and put out the Amorites that dwelt therein.
Zidzukulu za Makiri mwana wa Manase zinapita ku Giliyadi kulanda mzindawo ndi kuthamangitsira kunja Aamori omwe anali kumeneko.
40 Then Moses gaue Gilead vnto Machir the sonne of Manasseh, and he dwelt therein.
Tsono Mose anapereka Giliyadi kwa Amakiri, ana a Manase, ndipo anakhala kumeneko.
41 And Iair the sonne of Manasseh went and tooke the small townes thereof, and called them Hauoth Iair.
Yairi, mwana wa Manase analanda midzi yambiri ya Giliyadi ndi kuyitcha kuti Havoti-Yairi.
42 Also Nobah went and tooke Kenath, with the villages thereof and called it Nobah, after his owne name.
Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.