< Numbers 31 >

1 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Reuenge the children of Israel of the Midianites, and afterwarde shalt thou be gathered vnto thy people.
“Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
3 And Moses spake to the people, saying, Harnesse some of you vnto warre, and let them goe against Midian, to execute the vengeance of the Lord against Midian.
Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
4 A thousande of euery tribe throughout all the tribes of Israel, shall ye sende to the warre.
Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
5 So there were taken out of the thousands of Israel, twelue thousande prepared vnto warre, of euery tribe a thousand.
Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
6 And Moses sent them to the warre, euen a thousand of euery tribe, and sent them with Phinehas the sonne of Eleazar the Priest to the warre: and the holy instruments, that is, the trumpets to blow were in his hand.
Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
7 And they warred against Midian, as the Lord had commanded Moses, and slue all the males.
Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
8 They slue also the Kings of Midian among them that were slaine: Eui and Rekem, and Zur, and Hur and Reba fiue kings of Midian, and they slue Balaam the sonne of Beor with the sworde:
Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
9 But the children of Israel tooke the women of Midian prisoners, and their children, and spoyled all their cattell, and all their flockes, and all their goods.
Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
10 And they burnt all their cities, wherein they dwelt, and all their villages with fire.
Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
11 And they tooke all the spoyle and all the pray both of men and beastes.
Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
12 And they brought the captiues and that which they had taken, and the spoyle vnto Moses and to Eleazar the Priest, and vnto the Congregation of the children of Israel, into ye campe in the playne of Moab, which was by Iorden toward Iericho.
Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
13 Then Moses and Eleazar the Priest, and all the princes of the Congregation went out of the campe to meete them.
Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
14 And Moses was angry with the captaines of the hoste, with the captaines ouer thousands, and captaines ouer hundreds, which came from the warre and battel.
Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
15 And Moses sayde vnto them, What? haue ye saued all the women?
Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
16 Behold, these caused the children of Israel through the counsell of Balaam to commit a trespasse against the Lord, as concerning Peor, and there came a plague among the Congregation of the Lord.
Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
17 Now therefore, slay all the males among the children, and kill all the women that haue knowen man by carnall copulation.
Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
18 But all the women children that haue not knowen carnall copulation, keepe aliue for your selues.
koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
19 And ye shall remaine without the host seuen dayes, all that haue killed any person, and all that haue touched any dead, and purifie both your selues and your prisoners the third day and the seuenth.
“Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
20 Also ye shall purifie euery garment and all that is made of skins and al worke of goates heare, and all things made of wood.
Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
21 And Eleazar ye Priest sayd vnto the men of warre, which went to the battel, This is the ordinance of the law which the Lord commanded Moses,
Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
22 As for gold, and siluer, brasse, yron, tynne, and lead:
Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
23 Euen all that may abide the fire, yee shall make it goe through the fire, and it shalbe cleane: yet, it shalbe purified with the water of purification: and all that suffereth not the fire, yee shall cause to passe by the water.
ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
24 Ye shall wash also your clothes the seuenth day, and ye shalbe cleane: and afterward ye shall come into the Hoste.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
25 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
26 Take the summe of the praie that was taken, both of persons and of cattell, thou and Eleazar the Priest, and the chiefe fathers of the Congregation.
“Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
27 And deuide the praye betweene the souldiers that went to the warre, and all the Congregation.
Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
28 And thou shalt take a tribute vnto ye Lord of the men of warre, which went out to battel: one person of fiue hundreth, both of the persons, and of the beeues, and of the asses, and of the sheepe.
Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
29 Yee shall take it of their halfe and giue it vnto Eleazar the Priest, as an heaue offring of the Lord.
Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
30 But of the halfe of the children of Israel thou shalt take one, taken out of fiftie, both of the persons, of the beeues, of the asses, and of the sheepe, euen of all the cattel: and thou shalt giue them vnto the Leuites, which haue the charge of the Tabernacle of the Lord.
Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
31 And Moses and Eleazar the priest did as the Lord had commanded Moses.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
32 And the bootie, to wit, the rest of the praie which the men of warre had spoyled, was sixe hundreth seuentie and fiue thousand sheepe,
Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
33 And seuentie and two thousand beeues,
Ngʼombe 72,000,
34 And three score and one thousand asses,
abulu 61,000,
35 And two and thirtie thousande persons in all, of women that had lyen by no man.
ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
36 And the halfe, to wit, the part of them that went out to warre touching the nomber of sheepe, was three hundreth seuen and thirtie thousand, and fiue hundreth.
Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
37 And the Lordes tribute of the sheepe was sixe hundreth and seuentie and fiue:
mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
38 And the beeues were six and thirty thousad, whereof the Lordes tribute was seuentie and two.
ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
39 And the asses were thirtie thousande and fiue hundreth, whereof the Lordes tribute was three score and one:
abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
40 And of persons sixtene thousand, whereof the Lordes tribute was two and thirtie persons.
anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
41 And Moses gaue the tribute of the Lordes offring vnto Eleazar the Priest, as the Lord had commanded Moses.
Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
42 And of the halfe of the children of Israel, which Moses deuided from the men of warre,
Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
43 (For the halfe that perteined vnto the Congregation, was three hundreth thirtie and seuen thousand sheepe and fiue hundreth,
Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
44 And sixe and thirtie thousand beeues,
ngʼombe 36,000,
45 And thirtie thousand asses, and fiue hudreth,
abulu 30,500,
46 And sixteene thousande persons)
anthu 16,000.
47 Moses, I say, tooke of the halfe that perteined vnto the children of Israel, one taken out of fiftie, both of the persons, and of the cattell, and gaue them vnto the Leuites, which haue the charge of the Tabernacle of the Lord, as the Lord had commanded Moses.
Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
48 Then the captaines which were ouer thousandes of the hoste, the captaines ouer the thousandes, and the captaines ouer the hundreds came vnto Moses:
Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
49 And saide to Moses, Thy seruants haue taken the summe of the men of warre which are vnder our authoritie, and there lacketh not one man of vs.
iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
50 We haue therefore brought a present vnto the Lord, what euery man found of iewels of golde, bracelets, and cheines, rings, eare ringes, and ornaments of the legges, to make an atonement for our soules before the Lord.
Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
51 And Moses and Eleazar the Priest tooke the golde of them, and all wrought iewels,
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
52 And all the golde of the offring that they offered vp to the Lord (of the captaines ouer thousands and hundreds) was sixteene thousande seuen hundreth and fiftie shekels,
Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
53 (For the men of warre had spoyled, euery man for him selfe)
Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
54 And Moses and Eleazar the Priest tooke the golde of the captaines ouer the thousandes, and ouer the hundreds, and brought it into the Tabernacle of the Congregation, for a memoriall of the children of Israel before the Lord.
Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.

< Numbers 31 >