< Numbers 26 >

1 And so after the plague, the Lord spake vnto Moses, and to Eleazar the sonne of Aaron the Priest, saying,
Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni,
2 Take the nomber of all the Congregation of the children of Israel from twentie yeere olde and aboue throughout their fathers houses, all that go forth to warre in Israel.
“Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.”
3 So Moses and Eleazar the Priest spake vnto them in the plaine of Moab, by Iorden towarde Iericho, saying,
Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti,
4 From twentie yeere olde and aboue ye shall nomber the people, as the Lord had commanded Moses, and the childre of Israel, when they came out of the land of Egypt.
“Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.” Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:
5 Reuben the first borne of Israel: the children of Reube were: Hanoch, of whom came the familie of the Hanochites, and of Pallu the familie of the Palluites:
Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi: kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki; kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;
6 Of Hesron, the familie of the Hesronites: of Carmi, the familie of the Carmites.
kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.
7 These are the families of the Reubenites: and they were in nomber three and fourtie thousand, seuen hundreth and thirtie.
Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.
8 And the sonnes of Pallu, Eliab:
Mwana wa Palu anali Eliabu,
9 And the sonnes of Eliab, Nemuel, and Dathan, and Abiram: this Dathan and Abiram were famous in the Congregation, and stroue against Moses and against Aaron in the assemblie of Korah, when they stroue against the Lord.
ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova.
10 And the earth opened her mouth, and swalowed them vp with Korah, when the Congregation died, what time the fire consumed, two hundreth and fiftie men, who were for a signe.
Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo.
11 Notwithstanding, all the sonnes of Korah dyed not.
Koma ana a Kora sanafe nawo.
12 And the children of Simeon after their families were: Nemuel, of whom came the familie of the Nemuelites: of Iamin, the familie of the Iaminites: of Iachin, the familie of the Iachinites:
Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele; kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini; kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;
13 Of Zerah, the familie of the Zarhites: of Shaul, the familie of the Shaulites.
kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera; kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.
14 These are the families of the Simeonites: two and twentie thousand and two hundreth.
Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.
15 The sonnes of Gad after their families were: Zephon, of whome came ye familie of the Zephonites: of Haggi, the familie of the Haggites: of Shuni, the familie of the Shunites:
Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi: kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni; kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi; kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;
16 Of Ozni, the familie of the Oznites: of Eri, the familie of the Erites:
kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini; kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;
17 Of Arod, the familie of the Arodites: of Areli, the familie of the Arelites.
kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi; kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.
18 These are the families of the sonnes of Gad, according to their nombers, fourtie thousand and fiue hundreth.
Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.
19 The sonnes of Iudah, Er and Onan: but Er and Onan died in the land of Canaan.
Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.
20 So were the sonnes of Iudah after their families: of Shelah came the familie of ye Shelanites: of Pharez, the familie of the Pharzites, of Zerah, the familie of the Zarhites.
Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Sela, fuko la Asera; kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi; kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.
21 And the sonnes of Pharez were: of Hesron, the familie of the Hesronites: of Hamul, the familie of the Hamulites.
Zidzukulu za Perezi zinali izi: kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.
22 These are the families of Iudah, after their nombers, seuentie and sixe thousande and fiue hundreth.
Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.
23 The sonnes of Issachar, after their families were: Tola, of whom came the familie of the Tolaites: of Pua, the familie of the Punites:
Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Tola, fuko la Atola; kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;
24 Of Iashub the familie of the Iashubites: of Shimron, the familie of the Shimronites.
kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu. Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.
25 These are the families of Issachar, after their nombers, threescore and foure thousand and three hundreth.
Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.
26 The sonnes of Zebulun, after their families were: of Sered, the familie of the Sardites: of Elon, the familie of the Elonites: of Iahleel, the familie of the Iahleelites.
Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi; kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni; kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.
27 These are the families of the Zebulunites, after their nombers, three score thousande and fiue hundreth.
Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.
28 The sonnes of Ioseph, after their families were Manasseh and Ephraim.
Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:
29 The sonnes of Manasseh were: of Machir, the familie of the Machirites: and Machir begate Gilead: of Gilead came the familie of the Gileadites.
Zidzukulu za Manase: kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi); kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.
30 These are the sonnes of Gilead: of Iezer, the familie of the Iezerites: of Helek, the familie of the Helekites.
Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi; kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri; kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;
31 Of Asriel, the familie of the Asrielites: of Shechem, the familie of Shichmites.
kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli; kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;
32 Of Shemida, the familie of the Shemidaites: of Hepher, the familie of the Hepherites.
kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida; kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.
33 And Zelophehad the sonne of Hepher had no sonnes, but daughters: and the names of the daughters of Zelophehad were Mahlah, and Noah, Hoglah, Milcah and Tirzah.
(Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)
34 These are the families of Manasseh, and the nomber of them, two and fiftie thousand and seuen hundreth.
Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.
35 These are the sonnes of Ephraim after their families: of Shuthelah came the familie of the Shuthalhites: of Becher, the familie of the Bachrites: of Tahan, the familie of the Tahanites.
Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi; kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela; kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri; kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.
36 And these are the sonnes of Shuthelah: of Eran the familie of the Eranites.
Zidzukulu za Sutela zinali izi: kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.
37 These are the families of the sonnes of Ephraim after their nombers, two and thirtie thousand and fiue hundreth. these are the sonnes of Ioseph after their families.
Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500. Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.
38 These are the sonnes of Beniamin after their families: of Bela came the familie of the Belaites: of Ashbel, the familie of the Ashbelites: of Ahiram, the familie of the Ahiramites:
Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Bela, fuko la Abela; kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli; kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;
39 Of Shupham, the familie of the Suphamites: of Hupham, the familie of the Huphamites.
kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu; kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;
40 And the sonnes of Bela were Ard and Naaman: of Ard came the familie of the Ardites, of Naaman, the familie of the Naamites.
Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi: kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi; kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;
41 These are the sonnes of Beniamin after their families, and their nombers, fiue and fourtie thousand and sixe hundreth.
Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.
42 These are the sonnes of Dan after their families: of Shuham came the familie of the Shuhamites: these are the families of Dan after their housholdes.
Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu. Izi zinali zidzukulu za Dani.
43 All the families of the Shuhamites were after their nombers, threescore and foure thousand, and foure hundreth.
Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.
44 The sonnes of Asher after their families were: of Iimnah, the familie of the Iimnites: of Isui, the familie of the Isuites: of Beriah, the familie of the Berijtes.
Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna; kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi; kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;
45 The sonnes of Beriah were, of Heber the familie of the Heberites: of Malchiel, the familie of the Malchielites.
ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya: kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi; kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;
46 And the name of the daughter of Asher was Sarah.
(Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)
47 These are the families of the sonnes of Asher after their nombers, three and fifty thousand and foure hundreth.
Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.
48 The sonnes of Naphtali, after their families were: of Iahzeel, the families of the Iahzeelites: of Guni, the familie of the Gunites.
Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli; kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;
49 Of Iezer, the familie of the Izrites: of Shillem, the familie of the Shillemites.
kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri; kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.
50 These are the families of Naphtali according to their housholdes, and their nomber, fiue and fourtie thousande and foure hundreth.
Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.
51 These are the nombers of the children of Israel: sixe hundreth and one thousand, seuen hundreth and thirtie.
Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.
52 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
53 Vnto these the land shalbe deuided for an inheritance, according to the nomber of names.
“Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo.
54 To many thou shalt giue the more inheritance, and to fewe thou shalt giue lesse inheritance: to euery one according to his nomber shalbe giuen his inheritance.
Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa.
55 Notwithstanding, the land shalbe deuided by lot: according to the names of the tribes of their fathers they shall inherite:
Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo.
56 According to the lot shall the possession thereof be deuided betweene many and fewe.
Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”
57 These also are the nobers of ye Leuites, after their families: of Gershon came ye familie of the Gershonites: of Kohath, ye familie of the Kohathites: of Merari, the familie of the Merarites.
Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa: kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni; kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati; kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.
58 These are the families of Leui, the familie of the Libnites: the familie of the Hebronites: the familie of the Mahlites: the familie of the Mushites: the familie of the Korhites: and Kohath begate Amram.
Awanso anali mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, fuko la Kora banja la Akohati, (Kohati anali abambo a Amramu.
59 And Amrams wife was called Iochebed the daughter of Leui, which was borne vnto Leui in Egypt: and she bare vnto Amram Aaron, and Moses, and Miriam their sister.
Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.
60 And vnto Aaron were borne Nadab, and Abihu, Eleazar, and Ithamar.
Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
61 And Nadab and Abihu dyed, because they offred strange fire before the Lord.
Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).
62 And their nombers were three and twentie thousand, all males from a moneth old and aboue: for they were not nombred among the children of Israel, because there was none inheritance giuen them among the children of Israel.
Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.
63 These are the nombers of Moses and Eleazar the Priest which nombred the children of Israel in the plaine of Moab, neere Iorden, towarde Iericho.
Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.
64 And among these there was not a man of them, whome Moses and Aaron the Priest nobred, when they tolde the children of Israel in the wildernes of Sinai.
Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai;
65 For the Lord said of them, They shall die in the wildernes: so there was not left a man of them, saue Caleb the sonne of Iephunneh, and Ioshua the sonne of Nun.
Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.

< Numbers 26 >