< Numbers 25 >

1 Nowe whiles Israel abode in Shittim, the people began to commit whoredome with the daughters of Moab:
Aisraeli akukhala ku Sitimu, anayamba kuchita chigololo ndi akazi a ku Mowabu,
2 Which called the people vnto the sacrifice of their gods, and the people ate, and bowed downe to their gods.
amene ankawayitana ku nsembe za milungu yawo. Anthuwo anadya chakudya chopereka kwa milungu ndi kupembedza milunguyo.
3 And Israel coupled himselfe vnto Baal Peor: wherefore the wrath of the Lord was kindled against Israel:
Motero Aisraeli anapembedza nawo Baala-Peori ndipo Yehova anawapsera mtima kwambiri.
4 And the Lord sayde vnto Moses, Take all the heades of the people, and hang them vp before the Lord against ye sunne, that the indignation of the Lords wrath may be turned from Israel.
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga atsogoleri onse a anthu awa, uwaphe poyera, pamaso pa Yehova kuti mkwiyo waukulu wa Yehova uchoke pa Israeli.”
5 Then Moses sayd vnto the Iudges of Israel, Euery one slay his men that were ioyned vnto Baal Peor.
Choncho Mose anawuza oweruza a Israeli kuti, “Aliyense wa inu ayenera kupha anthu ake amene anapembedza nawo Baala-Peori.”
6 And behold, one of the children of Israel came and brought vnto his brethren a Midianitish woman in the sight of Moses, and in the sight of all the Congregation of the children of Israel, who wept before the doore of the Tabernacle of the Congregation.
Kenaka mwamuna wina wa ku Israeli anabweretsa ku banja lake mkazi wa Chimidiyani pamaso pa Mose ndi anthu onse a Israeli pamene ankalira pa khomo la tenti ya msonkhano.
7 And when Phinehas the sonne of Eleazar the sonne of Aaron the Priest sawe it, hee rose vp from the middes of the Congregation, and tooke a speare in his hand,
Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni ataona izi, anachoka pa msonkhanowo, natenga mkondo mʼdzanja lake.
8 And followed ye man of Israel into the tent, and thrust them both through: to wit, the man of Israel, and the woman, through her belly: so the plague ceased from the children of Israel.
Ndipo anatsatira Mwisraeliyu mpaka mʼtenti yake. Anasolola mkondowo ndi kubaya awiriwo kupyola Mwisraeliyo mpaka mʼthupi la mkaziyo. Pamenepo mliri unaleka pakati pa Aisraeli.
9 And there died in that plague, foure and twentie thousand.
Pa mliriwo, anthu okwana 24,000 anafa.
10 Then the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
11 Phinehas the sonne of Eleazar, the sonne of Aaron the Priest, hath turned mine anger away from the children of Israel, while hee was zealous for my sake among them: therefore I haue not consumed the children of Israel in my ielousie.
“Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni wabweza mkwiyo wanga pa Aisraeli chifukwa sanalole kuti wina aliyense apembedze mulungu wina koma Ine ndekha. Nʼchifukwa chake sindinawawononge mu mkwiyo wanga.
12 Wherefore say to him, Beholde, I giue vnto him my couenant of peace,
Tsono muwuze kuti ndikhazikitsa pangano langa la mtendere ndi iye.
13 And he shall haue it, and his seede after him, euen the couenant of the priestes office for euer, because he was zealous for his God, and hath made an atonement for the children of Israel.
Ndikupangana naye pangano la unsembe wosatha, iyeyo pamodzi ndi zidzukulu zake zonse, chifukwa sanalole kuti anthu awukire Ine Mulungu, ndipo anachita ntchito yopepesera machimo Aisraeli.”
14 And the name of the Israelite thus slayne, which was killed with the Midianitish woman, was Zimri the sonne of Salu, prince of the familie of the Simeonites.
Dzina la Mwisraeli yemwe anaphedwa ndi mkazi wa Chimidiyani anali Zimuri mwana wa Salu, mtsogoleri wa banja la Simeoni.
15 And the name of the Midianitish woman, that was slayne, was Cozbi the daughter of Zur, who was head ouer the people of his fathers house in Midian.
Ndipo dzina la mkazi wa Chimidiyani, yemwe anaphedwayo, linali Kozibi mwana wa Zuri, mtsogoleri wa fuko la ku Midiyaniko.
16 Againe ye Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
17 Vexe the Midianites, and smite them:
“Amidiyani ndi adani anu ndipo uwaphe,
18 For they trouble you with their wiles, wherewith they haue beguiled you as concerning Peor, and as concerning their sister Cozbi ye daughter of a prince of Midian, which was slayne in the day of the plague because of Peor.
chifukwa ankakuonani inu ngati adani awo pamene anakupusitsani pa nkhani ya ku Peori, ndiponso za mlongo wawo Kozibi, mwana wamkazi wa mtsogoleri wa Amidiyani, mkazi yemwe anaphedwa pamene mliri unabwera chifukwa cha zimene zinachitika ku Peori.”

< Numbers 25 >