< Numbers 22 >
1 After, the children of Israel departed and pitched in the plaine of Moab on the other side of Iorden from Iericho.
Aisraeli anayenda kupita ku zigwa za Mowabu nakamanga misasa yawo tsidya lina la Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
2 Now Balak the sonne of Zippor sawe all that Israel had done to the Amorites.
Tsono Balaki mwana wa Zipori anaona zonse zimene Aisraeli anachitira Aamori,
3 And the Moabites were sore afraide of the people, because they were many, and Moab fretted against the children of Israel.
ndipo Amowabu anaopa anthuwo chifukwa analipo ambiri. Amowabuwo anachita mantha kwambiri mpaka ananjenjemera chifukwa cha Aisraeli.
4 Therfore Moab said vnto the Elders of Midian, Nowe shall this multitude licke vp all that are round about vs, as an oxe licketh vp ye grasse of the fielde: and Balak the sonne of Zippor was King of the Moabites at that time.
Iwo anati kwa akuluakulu a ku Midiyani, “Gulu ili lidzabudula zonse zimene zatizungulira monga momwe ngʼombe yothena imathera udzu wa ku tchire.” Tsono Balaki mwana wa Zipori, yemwe anali mfumu ya Mowabu pa nthawi imeneyo,
5 Hee sent messengers therefore vnto Balaam the sonne of Beor to Pethor (which is by the riuer of the lande of the children of his folke) to call him, saying, Beholde, there is a people come out of Egypt, which couer the face of the earth, and lye ouer against me.
anatumiza amithenga kwa Balaamu mwana wa Beori, yemwe anali ku Petori, pafupi ndi mtsinje, mʼdziko la kwawo kuti akamuyitane. Balaki anati: “Taonani, anthu ochokera ku Igupto abwera, adzaza dziko lonse ndipo akufuna kuchita nane nkhondo.
6 Come now therefore, I pray thee, and curse me this people (for they are stronger then I) so it may be that I shall be able to smite them, and to driue them out of the land: for I knowe that hee, whome thou blessest, is blessed, and he whom thou cursest, shall be cursed.
Tsopano bwera, utemberere anthu amenewa chifukwa ndi amphamvu kwambiri kuposa ine. Mwina ndingadzawagonjetse ndi kuwatulutsira kunja kwa dzikoli chifukwa ndikudziwa kuti amene umawadalitsa amadalitsika, ndipo amene umawatemberera amatembereredwa.”
7 And the Elders of Moab, and the Elders of Midian departed, hauing the reward of the soothsaying in their hande, and they came vnto Balaam, and tolde him the wordes of Balak.
Akuluakulu a Mowabu ndi akuluakulu a Midiyani ananyamuka atatenga ndalama zokalipirira mawula. Atafika kwa Balaamu, anamuwuza zomwe Balaki ananena.
8 Who answered them, Tary here this night, and I will giue you an answere, as the Lord shall say vnto mee. So the princes of Moab abode with Balaam.
Balaamu anawawuza kuti, “Mugone konkuno usiku uno, ndipo ndikuyankhani zomwe Yehova andiwuze.” Choncho akuluakulu a Amowabu anagona kwa Balaamu.
9 Then God came vnto Balaam, and sayde, What men are these with thee?
Mulungu anabwera kwa Balaamu namufunsa kuti, “Kodi anthu ali ndi iwewa ndani?”
10 And Baalam said vnto God, Balak ye sonne of Zippor, king of Moab hath set vnto me, saying,
Balaamu anayankha Mulungu kuti, “Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, ananditumizira uthenga uwu:
11 Beholde, there is a people come out of Egypt and couereth the face of the earth: come nowe, curse them for my sake: so it may be that I shalbe able to ouercome them in battell, and to driue them out.
‘Taonani, anthu amene achokera ku dziko la Igupto adzaza dziko lonse. Tsopano bwera udzawatemberere mʼmalo mwanga. Mwina ndidzatha kumenyana nawo ndi kuwatulutsa.’”
12 And God said vnto Balaam, Go not thou with them, neither curse the people, for they are blessed.
Koma Mulungu anawuza Balaamu kuti, “Usapite nawo. Usawatemberere anthu amenewo chifukwa ndi odalitsika.”
13 And Balaam rose vp in the morning, and sayde vnto ye princes of Balak, Returne vnto your land: for the Lord hath refused to giue me leaue to go with you.
Mmawa mwake Balaamu anadzuka ndi kuwuza akuluakulu a Balaki aja kuti, “Bwererani ku dziko la kwanu chifukwa Yehova sanandilole kuti ndipite nanu.”
14 So the princes of Moab rose vp, and went vnto Balak, and sayd, Balaam hath refused to come with vs.
Kotero akuluakulu a Mowabu anabwerera kwa Balaki ndi kukanena kuti, “Balaamu wakana kubwera nafe.”
15 Balak yet sent againe moe princes, and more honourable then they.
Kenaka Balaki anatumanso akuluakulu ena ambiri ndi olemekezeka kwambiri kuposa oyamba aja ndipo
16 Who came to Balaam, and sayde to him, Thus saith Balak the sonne of Zippor, Bee not thou staied, I pray thee, from comming vnto me.
anafika kwa Balaamu nati; “Zomwe Balaki mwana wa Zipori akunena ndi izi: ‘Usalole kuti china chilichonse chikulepheretse kubwera kwa ine,
17 For I wil promote thee vnto great honour, and wil do whatsoeuer thou sayest vnto me: come therefore, I pray thee, curse me this people.
chifukwa ndidzakulipira bwino kwambiri ndipo ndidzakuchitira chilichonse chimene unganene. Bwera ndipo uwatemberere anthu amenewa mʼmalo mwanga.’”
18 And Balaam answered, and sayde vnto the seruants of Balak, If Balak woulde giue me his house full of siluer and golde, I can not goe beyonde the worde of the Lord my God, to doe lesse or more.
Koma Balaamu anayankha atumiki a Balaki kuti, “Ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingachite chilichonse chachikulu kapena chachingʼono kuposa kuchita lamulo la Yehova Mulungu wanga.
19 But nowe, I pray you, tary here this night, that I may wit, what the Lord will say vnto mee more.
Tsopano mukhale kuno usiku uno monga ena anachitira, ndidzaona chimene Yehova adzandiwuza.”
20 And God came vnto Balaam by night, and sayd vnto him, If the men come to call thee, rise vp, and goe with them: but onely what thing I say vnto thee, that shalt thou doe.
Usiku umenewo Mulungu anabwera kwa Balaamu ndipo anati, “Popeza anthu awa abwera kudzakuyitana, nyamuka, pita nawo koma ukachite zokhazo zimene ndikuwuze.”
21 So Balaam rose vp early, and sadled his asse, and went with the princes of Moab.
Balaamu anadzuka mmawa, namanga bulu wake wamkazi ndipo anapita ndi akuluakulu a Mowabu.
22 And ye wrath of God was kindled, because he went: and the Angel of the Lord stood in the way to be against him, as he rode vpon his asse, and his two seruants were with him.
Koma Mulungu anakwiya kwambiri pamene ankapita ndipo mngelo wa Yehova anayima pa njira kutsutsana naye. Balaamu anakwera bulu wake wamkazi ndipo antchito ake awiri anali naye.
23 And when the asse saw the Angel of the Lord stand in the way, and his sworde drawen in his hand, the asse turned out of the way and went into the field, but Balaam smote the asse, to turne her into the way.
Pamene buluyo anaona mngelo wa Yehova atayima pa njira ndi lupanga mʼmanja mwake, anapatukira kumbali kwa msewu napita kutchire. Balaamu anamumenya kuti abwerere mu msewu.
24 Againe the Angel of the Lord stood in a path of the vineyardes, hauing a wall on the one side, and a wall on the other.
Kenaka mngelo wa Yehova anayima mʼkanjira kakangʼono pakati pa minda iwiri ya mpesa yokhala ndi makoma mbali zonse
25 And when the asse sawe the Angel of the Lord, she thrust her selfe vnto the wall, and dasht Balaams foote against the wall: wherefore hee smote her againe.
Bulu uja ataona mngelo wa Yehova anadzipanikiza ku khoma, kukhukhuza phazi la Balaamu kukhomako. Ndipo pomwepo Balaamu anamenya buluyo kachiwiri.
26 Then the Angel of the Lord went further, and stoode in a narowe place, where was no way to turne, either to the right hand, or to the left.
Kenaka mngelo wa Yehova anapita patsogolo ndi kuyima pamalo opanikizika pomwe panalibe poti nʼkutembenukira ku dzanja lamanja kapena lamanzere.
27 And when the asse sawe the Angell of the Lord, she lay downe vnder Balaam: therefore Balaam was very wroth, and smote the asse with a staffe.
Buluyo ataonanso mngelo wa Yehova uja, anagona pansi Balaamu ali pa msana, ndipo iye anakwiya ndi kumumenya ndi ndodo yake.
28 Then the Lord opened the mouth of the asse, and she saide vnto Balaam, What haue I done vnto thee, that thou hast smitten me nowe three times?
Pamenepo Yehova anayankhulitsa bulu uja, ndipo buluyo anati kwa Balaamu, “Ndakuchitirani chiyani kuti mundimenye katatuka?”
29 And Balaam saide vnto the asse, Because thou hast mocked me: I woulde there were a sworde in mine hand, for nowe would I kill thee.
Balaamu anati kwa buluyo, “Wandipusitsa, ndikanakhala ndi lupanga mʼmanja mwanga, ndikanakupha pomwe pano.”
30 And the asse saide vnto Balaam, Am not I thine asse, which thou hast ridden vpon since thy first time vnto this day? haue I vsed at any time to doe thus vnto thee? Who said, Nay.
Buluyo anati kwa Balaamu, “Kodi sindine bulu wanu, amene mumakwera nthawi zonse kufikira lero? Kodi ndinakuchitiranipo zoterezi?” Iye anati “Ayi.”
31 And the Lord opened the eyes of Balaam, and he sawe the Angel of the Lord standing in the way with his sword drawen in his hande: then he bowed him selfe, and fell flat on his face.
Pomwepo Yehova anatsekula maso Balaamu ndipo anaona mngelo wa Yehovayo ali chiyimire pa njira ndi lupanga losolola. Tsono iye anawerama nalambira pamaso pake.
32 And the Angel of the Lord said vnto him, Wherefore hast thou nowe smitten thine asse three times? beholde, I came out to withstande thee, because thy way is not straight before me.
Mngelo wa Yehova anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani wamenya bulu wako katatu? Taona, Ine ndabwera kudzakutsutsa chifukwa ulendo wakowu ndi woyipa pamaso panga.
33 But the asse sawe me, and turned from me now three times: for els, if she had not turned from me, surely I had euen nowe slaine thee, and saued her aliue.
Buluyu anandiona ndi kupatuka katatu aka. Akanakhala kuti sanapatuke, ndikanakupha tsopano, koma buluyu nʼkanamusiya ndi moyo.”
34 Then Balaam saide vnto the Angel of the Lord, I haue sinned: for I wist not that thou stoodest in the way against me: now therefore if it displease thee, I will turne home againe.
Balaamu anati kwa mngelo wa Yehova uja, “Ndachimwa. Sindinadziwe kuti munayima pa njira kunditsutsa. Tsopano ngati Inu simunakondwe, ineyo ndibwerera.”
35 But the Angel said vnto Balaam, Go with the men: but what I say vnto thee, that shalt thou speake. So Balaam went with ye princes of Balak.
Mngelo wa Yehova anati kwa Balaamu, “Pita ndi anthuwa koma ukayankhule zokhazo zimene ndikakuwuze.” Choncho Balaamu anapita ndi akuluakulu a Balaki.
36 And when Balak heard that Balaam came, he went out to meete him vnto a citie of Moab, which is in the border of Arnon, euen in the vtmost coast.
Balaki atamva kuti Balaamu akubwera, anapita kukakumana naye ku mzinda wa Mowabu umene unali mʼmalire a Arinoni, mʼmphepete mwa dziko lake.
37 Then Balak saide vnto Balaam, Did I not sende for thee to call thee? Wherefore camest thou not vnto me? am I not able in deede to promote thee vnto honour?
Balaki anati kwa Balaamu, “Kodi sindinakutumizire uthenga woti ubwere msanga? Chifukwa chiyani sunabwere kwa ine? Kodi sindingathe kukulipira mokwanira?”
38 And Balaam made answere vnto Balak, Lo, I am come vnto thee, and can I nowe say any thing at all? the worde that God putteth in my mouth, that shall I speake.
Balaamu anayankha Balaki kuti, “Taonani, ndabwera kwa inu lero, kodi ine ndili ndi mphamvu zoti nʼkuyankhula chilichonse? Inetu ndiyenera kuyankhula zokhazo zimene Mulungu wandiwuza.”
39 So Balaam went with Balak, and they came vnto the citie of Huzoth.
Pamenepo Balaamu anapita pamodzi ndi Balaki ku Kiriati-Huzoti.
40 Then Balak offred bullockes, and sheepe, and sent thereof to Balaam, and to the princes that were with him.
Balaki anapereka nsembe ngʼombe ndi nkhosa, ndipo anapereka zina kwa Balaamu ndi kwa akuluakulu omwe anali naye.
41 And on the morowe Balak tooke Balaam, and brought him vp into the hie places of Baal, that thence hee might see the vtmost part of the people.
Mmawa mwake Balaki anatenga Balaamu napita limodzi ku Bamoti Baala, ndipo kumeneko anakaonako gulu lina la Aisraeliwo.