< Numbers 17 >

1 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Speake vnto the children of Israel, and take of euery one of them a rod, after the house of their fathers, of all their princes according to the familie of their fathers, euen twelue rods: and thou shalt write euery mans name vpon his rod.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake.
3 And write Aarons name vpon the rod of Leui: for euery rodde shalbe for the head of the house of their fathers.
Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse.
4 And thou shalt put them in the Tabernacle of the Congregation, before the Arke of the Testimonie, where I wil declare my selfe to you.
Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe.
5 And the mans rod, whome I chuse, shall blossome: and I will make cease from mee the grudgings of the children of Israel, which grudge against you.
Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”
6 Then Moses spake vnto the children of Israel, and al their princes gaue him a rod, one rod for euery Prince, according to the houses of their fathers, euen twelue rods, and the rod of Aaron was among their roddes.
Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo.
7 And Moses layde the rods before the Lord in the Tabernacle of the Testimonie.
Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.
8 And when Moses on the morow went into the Tabernacle of the Testimonie, beholde, the rod of Aaron for the house of Leui was budded, and brought forth buddes, and brought forth blossoms, and bare ripe almondes.
Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi.
9 Then Moses brought out all the rods from before the Lord vnto all the children of Israel: and they looked vpon them, and tooke euery man his rodde.
Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.
10 After, the Lord said vnto Moses, Bring Aarons rod againe before the Testimonie to bee kept for a token to the rebellious children, and thou shalt cause their murmurings to cease from me, that they dye not.
Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.”
11 So Moses did as the Lord had commanded him: so did he.
Mose anachita monga Yehova anamulamulira.
12 And the children of Israel spake vnto Moses, saying, Behold, we are dead, we perish, we are all lost:
Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika!
13 Whosoeuer commeth neere, or approcheth to the Tabernacle of the Lord, shall dye: shall we be consumed and dye?
Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”

< Numbers 17 >