< Nehemiah 6 >

1 And when Sanballat, and Tobiah, and Geshem the Arabian, and the rest of our enemies heard that I had built the wall, and that there were no more breaches therein, (though at that time I had not set vp the doores vpon the gates)
Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata.
2 Then sent Sanballat and Geshem vnto me, saying, Come thou that we may meete together in the villages in the plaine of Ono: and they thought to doe me euill.
Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.” Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko.
3 Therefore I sent messengers vnto them, saying, I haue a great worke to doe, and I can not come downe: why should the worke cease, whiles I leaue it, and come downe to you?
Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?”
4 Yet they sent vnto me foure times after this sort. And I answered them after the same maner.
Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.
5 Then sent Sanballat his seruant after this sorte vnto me the fift time, with an open letter in his hand,
Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata.
6 Wherein was written, It is reported among the heathen, and Gashmu hath sayd it, that thou and the Iewes thinke to rebel, for the which cause thou buildest the wall and thou wilt bee their King according to these wordes.
Mu kalatamo munali mawu akuti, “Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo.
7 Thou hast also ordeyned the Prophets to preach of thee at Ierusalem, saying, There is a King in Iudah: and nowe according to these wordes it shall come to the Kings eares: come now therefore, and let vs take counsell together.
Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”
8 Then I sent vnto him, saying, It is not done according to these wordes that thou sayest: for thou feynest them of thine owne heart.
Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”
9 For all they afrayed vs, saying, Their handes shalbe weakened from the worke, and it shall not be done: nowe therefore incourage thou me.
Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.” Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”
10 And I came to the house of Shemaiah the sonne of Delaiah the sonne of Mehetabeel, and he was shut vp, and he said, Let vs come together into the house of God in the middes of the Temple, and shut the doores of the Temple: for they will come to slay thee: yea, in the night will they come to kill thee.
Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”
11 Then I said, Should such a man as I, flee? Who is he, being as I am, that would go into the Temple to liue? I will not goe in.
Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!”
12 And loe, I perceiued, that God had not sent him, but that he pronounced this prophecie against me: for Tobiah and Sanballat had hired him.
Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi.
13 Therefore was he hyred, that I might be afrayde, and doe thus, and sinne, and that they might haue an euill report that they might reproche me.
Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.
14 My God, remember thou Tobiah, and Sanballat according vnto these their workes, and Noadiah the Prophetesse also, and the rest of the Prophets that would haue put me in feare.
Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”
15 Notwithstanding the wall was finished on the fiue and twentieth day of Elul, in two and fiftie dayes.
Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52.
16 And when all our enemies heard thereof, euen all the heathen that were about vs, they were afraid, and their courage failed them: for they knew, that this worke was wrought by our God.
Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.
17 And in these dayes were there many of the princes of Iudah, whose letters went vnto Tobiah, and those of Tobiah came vnto them.
Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo,
18 For there were many in Iudah, that were sworne vnto him: for he was the sonne in lawe of Shechaniah, the sonne of Arah: and his sonne Iehonathan had the daughter of Meshullam, the sonne of Berechiah.
pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya.
19 Yea, they spake in his praise before me, and tolde him my wordes, and Tobiah sent letters to put me in feare.
Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.

< Nehemiah 6 >