< Nahum 2 >
1 The destroyer is come before thy face: keepe the munition: looke to the way: make thy loynes strong: increase thy strength mightily.
Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
2 For the Lord hath turned away the glorie of Iaakob, as the glorie of Israel: for the emptiers haue emptied them out, and marred their vine branches.
Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
3 The shield of his mightie men is made red: the valiant men are in skarlet: the charets shalbe as in the fire and flames in the day of his preparation, and the firre trees shall tremble.
Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
4 The charets shall rage in the streetes: they shall runne to and from in the hie wayes: they shall seeme like lampes: they shall shoote like the lightning.
Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
5 He shall remember his strong men: they shall stumble as they goe: they shall make haste to the walles thereof, and the defence shall bee prepared.
Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
6 The gates of the riuers shalbe opened, and the palace shall melt.
Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
7 And Huzzab the Queene shalbe led away captiue, and her maides shall leade her as with the voyce of doues, smiting vpon their breastes.
Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
8 But Nineueh is of olde like a poole of water: yet they shall flee away. Stande, stande, shall they crie: but none shall looke backe.
Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
9 Spoyle ye the siluer, spoyle the golde: for there is none ende of the store, and glorie of all the pleasant vessels.
Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
10 She is emptie and voyde and waste, and the heart melteth, and the knees smite together, and sorowe is in all loynes, and the faces of the all gather blackenesse.
Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
11 Where is the dwelling of the lyons, and the pasture of the lyons whelpes? where the lyon, and the lionesse walked, and the lyons whelpe, and none made them afrayde.
Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
12 The lyon did teare in pieces ynough for his whelpes, and woryed for his lyonesse, and filled his holes with praye, and his dennes with, spoyle.
Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
13 Beholde, I come vnto thee, sayeth the Lord of hostes, and I will burne her charets in the smoke, and the sworde shall deuoure thy yong lyons, and I will cut off thy spoyle from the earth, and the voyce of thy messengers shall no more be heard.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”