< Micah 5 >

1 Nowe assemble thy garisons, O daughter of garisons: he hath layed siege against vs: they shall smite the iudge of Israel with a rod vpon the cheeke.
Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo, pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe. Adzakantha ndi ndodo pa chibwano cha wolamulira wa Israeli.
2 And thou Beth-leem Ephrathah art litle to bee among the thousandes of Iudah, yet out of thee shall he come forth vnto me, that shalbe the ruler in Israel: whose goings forth haue bene from the beginning and from euerlasting.
“Koma iwe Betelehemu Efurata, ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda, mwa iwe mudzatuluka munthu amene adzalamulira Israeli, amene chiyambi chake nʼchakalekale, nʼchamasiku amakedzana.”
3 Therefore will he giue them vp, vntill the time that shee which shall beare, shall trauaile: then the remnant of their brethren shall returne vnto the children of Israel.
Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire. Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
4 And he shall stand, and feed in the strength of the Lord, and in the maiestie of the Name of the Lord his God, and they shall dwel still: for now shall he be magnified vnto the ends of the world.
Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake mwa mphamvu ya Yehova, mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake. Ndipo iwo adzakhala mu mtendere, pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
5 And hee shall be our peace when Asshur shall come into our lande: when he shall tread in our palaces, then shall we raise against him seuen shepheardes, and eight principall men.
Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
6 And they shall destroy Asshur with the sword, and the land of Nimrod with their swordes: thus shall he deliuer vs from Asshur, when hee commeth into our lande, and when he shall tread within our borders.
Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga, dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo. Adzatipulumutsa kwa Asiriya akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu kudzatithira nkhondo.
7 And the remnant of Iaakob shalbe among many people, as a dewe from the Lord, and as the showres vpon the grasse, that waiteth not for man, nor hopeth in the sonnes of Adam.
Otsalira a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu ngati mame ochokera kwa Yehova, ngati mvumbi pa udzu, omwe sulamulidwa ndi munthu kapena kudikira lamulo la anthu.
8 And the remnant of Iaakob shalbe among the Gentiles in the middes of many people, as the lyon among the beastes of the forest, and as the lyons whelpe among the flockes of sheepe, who when he goeth thorow, treadeth downe and teareth in pieces, and none can deliuer.
Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu, mʼgulu la anthu a mitundu yambiri, ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango. Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa, amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula, ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
9 Thine hand shall bee lift vp vpon thine aduersaries, and all thine enemies shalbe cut off.
Mudzagonjetsa adani anu, ndipo adani anu onse adzawonongeka.
10 And it shall come to passe in that day, sayth the Lord, that I will cut off thine horses out of the middes of thee, and I will destroy thy charets.
Yehova akuti, “Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse ndi kuphwasula magaleta anu.
11 And I will cut off the cities of thy land, and ouerthrowe all thy strong holdes.
Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu ndi kugwetsa malinga anu onse.
12 And I will cut off thine enchanters out of thine hande: and thou shalt haue no more southsayers.
Ndidzawononga ufiti wanu ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
13 Thine idoles also will I cut off, and thine images out of the middes of thee: and thou shalt no more worship the woorke of thine hands.
Ndidzawononga mafano anu osema pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu; simudzagwadiranso zinthu zopanga ndi manja anu.
14 And I wil plucke vp thy groues out of the middes of thee: so will I destroy thine enemies.
Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu, ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
15 And I will execute a vegeance in my wrath and indignation vpon the heathen, which they haue not heard.
Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya mitundu imene sinandimvere Ine.”

< Micah 5 >