< Micah 2 >
1 Woe vnto them, that imagine iniquitie, and worke wickednesse vpon their beddes: when the morning is light they practise it because their hande hath power.
Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu, kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo! Kukacha mmawa amakachitadi chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.
2 And they couet fields, and take them by violence, and houses, and take them away: so they oppresse a man and his house, euen man and his heritage.
Amasirira minda ndi kuyilanda, amasirira nyumba ndi kuzilanda. Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo, munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.
3 Therefore thus saieth the Lord, Beholde, against this familie haue I deuised a plague, whereout yee shall not plucke your neckes, and ye shall not go so proudly, for this time is euill.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa, tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha. Inu simudzayendanso monyada, pakuti idzakhala nthawi ya masautso.
4 In that daye shall they take vp a parable against you, and lament with a dolefull lamentation, and say, We be vtterly wasted: hee hath changed the portion of my people: how hath he taken it away to restore it vnto mee? he hath deuided our fieldes.
Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe; adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro: ‘Tawonongeka kotheratu; dziko la anthu anga lagawidwa. Iye wandilanda! Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’”
5 Therefore thou shalt haue none that shall cast a corde by lot in the Congregation of the Lord.
Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova kuti agawe dziko pochita maere.
6 They that prophecied, Prophecie ye not. They shall not prophecie to them, neither shall they take shame.
Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere! Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi; ife sitidzachititsidwa manyazi.”
7 O thou that art named of the house of Iaakob, is the Spirite of the Lord shortened? are these his workes? are not my wordes good vnto him that walketh vprightly?
Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena: “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya? Kodi Iye amachita zinthu zotere?” “Kodi mawu ake sabweretsa zabwino kwa amene amayenda molungama?
8 But hee that was yesterday my people, is risen vp on the other side, as against an enemie: they spoyle the beautifull garment from them that passe by peaceably, as though they returned from the warre.
Posachedwapa anthu anga andiwukira ngati mdani. Mumawavula mkanjo wamtengowapatali anthu amene amadutsa mosaopa kanthu, monga anthu amene akubwera ku nkhondo.
9 The women of my people haue ye cast out from their pleasant houses, and from their childre haue ye taken away my glorie continually.
Mumatulutsa akazi a anthu anga mʼnyumba zawo zabwino. Mumalanda ana awo madalitso anga kosatha.
10 Arise and depart, for this is not your rest: because it is polluted, it shall destroy you, euen with a sore destruction.
Nyamukani, chokani! Pakuti ano si malo anu opumulirapo, chifukwa ayipitsidwa, awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.
11 If a man walke in the Spirit, and would lie falsely, saying, I wil prophecie vnto thee of wine, and of strong drinke, he shall euen be the prophet of this people.
Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti, ‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri, woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’
12 I will surely gather thee wholy, O Iaakob: I will surely gather the remnant of Israel: I will put them together as the sheepe of Bozrah, euen as the flocke in the mids of their folde: the cities shall be full of brute of the men.
“Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse; ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli. Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola, ngati ziweto pa msipu wake; malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.
13 The breaker vp shall come vp before them: they shall breake out, and passe by the gate, and goe out by it, and their King shall goe before them, and the Lord shalbe vpon their heades.
Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo; iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka. Mfumu yawo idzawatsogolera, Yehova adzakhala patsogolo pawo.”